Yes. 13 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kulangidwa kwa Babiloni

1 Yes. 47.1-15; Yer. 50.1—51.64 Nawu uthenga wonena za Babiloni umene Yesaya, mwana wa Amozi, adalandira kwa Mulungu.

2Kwezani mbendera yankhondo pa phiri loti see.

Muŵafuulire ankhondo ndi kuŵakodola

kuti adzaloŵe pa zipata za mzinda.

3Ine Mulungu mwini wake ndapereka

malamulo kwa anthu anga opatulika.

Ndasonkhanitsa ankhondo amphamvu,

amene amakondwerera kupambana kwanga,

kuti akhale zida zanga zolangira

amene ndimaŵakwiyira.

4Tamvani phokoso kumapiriku!

Likumveka ngati phokoso la chinamtindi cha anthu.

Imvani chiwawa m'maufumu!

Ndiye ngati mitundu ya anthu

ikusonkhana pamodzi.

Chauta Wamphamvuzonse akukhazika

ankhondo ake mokonzekera kumenya nkhondo.

5Iwowo akuchokera ku maiko akutali,

ku malekezero a dziko.

Ndiye kuti Chauta wanyamula zida

zake zija mokwiya,

akubwera kuti adzaononge dziko lonse lapansi.

6 Yow. 1.15 Lirani kwamphamvu pakuti tsiku

la Chauta layandikira.

Likubwera ndi chiwonongeko chochokera kwa Mphambe.

7Tsono manja onse adzafooka,

ndipo mtima wa munthu aliyense udzachokamo.

8Onse adzada nkhaŵa, adzavutika

ndi kumva zoŵaŵa,

zoŵaŵa zake zonga zimene amazimva mkazi pochira.

Azidzayang'anana mwamantha,

nkhope zao zidzagwa ndi manyazi.

9Zoonadi, tsiku la Chauta likudza,

tsiku lopanda chisoni,

laukali ndi lamkwiyo.

Chauta akubwera kuti asandutse dziko

lapansi chipululu ndi kuwononga

anthu ochimwa am'menemo.

10 Ezek. 32.7; Mt. 24.29; Mk. 13.24, 25; Lk. 21.25; Chiv. 6.12, 13; 8.12 Nyenyezi zonse zakumwamba

sizidzaonetsanso kuŵala.

Dzuŵa lidzada potuluka,

ndipo mwezi sudzaŵala konse.

11Chauta akuti,

“Ndidzalanga anthu a dziko lapansi

chifukwa cha kuipa kwao,

ndidzalanga oipa chifukwa cha kuchimwa kwao.

Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza

ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa

anthu ankhanza.

12Anthu ndidzaŵasandutsa

osapezekapezeka kuposanso m'mene

aliri golide wangwiro,

mtundu wa anthu udzakhala wosoŵa ngati

golide wa ku Ofiri.

13Tsono ndidzagwedeza mlengalenga,

ndipo dziko lapansi lidzachoka pa maziko ake.

Zonsezi zidzachitika chifukwa cha ukali

wa Ine Chauta Wamphamvuzonse pa tsiku

la mkwiyo wanga woopsa.

14Choncho munthu aliyense adzabwerera kwa anthu akwao,

aliyense adzathaŵira ku dziko lake,

ngati mbaŵala zothaŵa anthu auzimba

kapenanso ngati nkhosa zopanda wozikusa.

15Aliyense amene adzapezeke adzabayidwa chipyoza.

Aliyense amene adzagwidwe adzaphedwa ndi lupanga.

16Ana ao akhanda adzatswanyidwa iwo akuwona.

M'nyumba mwao mudzafunkhidwa,

ndipo akazi ao adzaŵachimwitsa mwakhakhamizo.

17“Ine Chauta ndidzadzutsa Amedi kuti

amenyane ndi Ababiloni.

Iwo safuna siliva

ndipo sakondwa ndi golide.

18Adzapha anyamata ndi mauta ao.

Sadzachitira chifundo ana.

Mitima yao siidzamva chisoni ndi ana akhanda omwe.

19 Gen. 19.24 Babiloni ufumu wake ndi waulemerero

kuposa maufumu ena onse,

ndipo anthu ake amaunyadira.

Koma Ine Chauta ndidzaononga

mzinda wa Babiloniwo

monga ndidaonongera Sodomu ndi Gomora

pa nthaŵi imene ndidagonjetsa mizindayo.

20Anthu sadzakhalamonso kapena kukhazikikamo

pa mibadwo yonse.

Mluya aliyense woyendayenda sadzamangako hema kumeneko,

abusa sadzaŵetako ziŵeto zao kumeneko.

21 Yes. 34.14; Zef. 2.14; Chiv. 18.2 Koma nyama zakuthengo ndizo zimene

zidzakhale kumeneko,

nyumba zake zidzadzaza ndi akadzidzi.

Kuzidzayendayenda nthiŵatiŵa,

ndipo atonde akuthengo azidzavinavinako.

22M'nsanja zake muzidzalira afisi,

m'nyumba zake zaufumu zokongola muzidzalira nkhandwe.

Nthaŵi yake yayandikira,

ndithu masiku ake ali pafupi kutha.”

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help