Mas. 6 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pemphero lopempha chithandizo pa nthaŵi yamavutoKwa Woimbitsa Nyimbo. Aimbire zipangizo zazingwe, zeze pamwamba. Salmo la Davide.

1 Mas. 38.1 Inu Chauta, musandikalipire ndi kundidzudzula,

musapse mtima ndi kundilanga.

2Ndichitireni chifundo, Inu Chauta,

chifukwa chakuti ndine wofooka.

Limbitseni, Inu Chauta,

chifukwa m'nkhongono mwanga mwaweyeseka.

3Mtima wanganso wazunzika kwambiri.

Nanga Inu Chauta,

zimenezi zidzakhala zikuchitika mpaka liti?

4Bwerani, Inu Chauta, mudzandilanditse.

Mundipulumutse

chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

5Anthu akufa sangathe kukutamandani ku manda.

M'dziko la akufa ndani angathe kukuyamikani?

6Ndatopa nkubuula kwambiri.

Ndimanyowetsa bedi langa ndi misozi

usiku uliwonse.

Ndimakhathamiza pogona panga

chifukwa cha kulira kwanga.

7Maso anga atupa chifukwa cha kulira,

afooka chifukwa cha adani anga onse.

8 Mt. 7.23; Lk. 13.27 Chokani apa, inu nonse ochita zoipa,

Chauta wamva kulira kwanga.

9Chauta wamva pemphero langa

ndipo wandiyankha.

10Adani anga onse adzagonjetsedwa mwa manyazi

ndipo adzagwidwa ndi mantha,

modzidzimuka onse adzathaŵa motaya mtima.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help