Mas. 129 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pemphero lopempha kuti adani a Israele alangidweNyimbo yoimba pokwera ku Yerusalemu.

1“Adani akhala akundizunza kwambiri

kuyambira unyamata wanga,”

Israele anene choncho tsopano,

2“Adani akhala akundizunza kwambiri

kuyambira unyamata wanga,

komabe sadandipambane.

3“Pondikwapula adani anga

adachita ngati kulima pamsana panga,

kulima mizere yaitali.”

4Koma Chauta ndi wolungama,

wandimasula zingwe za anthu oipa.

5Anthu onse odana ndi Ziyoni

agonjetsedwe ndi kupirikitsidwa mwamanyazi.

6Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba,

umene umafota usanakule.

7Woumweta sangadzaze nkumanja komwe,

womanga mitolo sangamange nchitsakato chomwe.

8Anthu odutsapo sadzanena kwa omwetawo kuti,

“Madalitso a Chauta akhale nanu.”

“Tikukudalitsani potchula dzina la Chauta.”

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help