1 Mphu. 16.3 Ndibwino koposa kukhala wosabereka
koma uli wachilungamo,
chifukwa kulungamako anthu amakukumbukira mpaka muyaya,
kumavomerezedwa ndi Mulungu ndi anthu omwe.
2Mkhalidwe wotere ukakhalapo, timautsanzira,
koma ukakhala palibe, timaulakalaka.
Mpaka muyaya udzayenda patsogolo,
utavala chisoti chaulemerero,
chifukwa udapambana pa nkhondo
ya kulimbana ndi zoipa.
3Koma ana ochuluka a anthu osamvera
adzakhala opandapake.
Poti adabadwira m'chigololo,
sadzazika mizu mozama,
sadzakhala ndi maziko olimba.
4Ngakhale aphuke nthambi pa kanthaŵi,
masinde ao osalimba adzagwedezeka ndi mphepo,
mphepo yamkuntho idzaŵazula.
5Nthambi zao zidzathyoka zisanakhwime,
zipatso zao zidzakhala zosadyeka,
chifukwa ndi zosapsa bwino
ndipo ndi zopandapake.
6Ana obadwira m'chigololo
amakhala mboni zotsutsa makolo ao
pamene Mulungu aweruza mlandu wao.
Kufa msanga kwa anthu olungama7Koma munthu wolungama,
ngakhale afe msanga,
adzapeza chiwuso.
8Timalemekeza nkhalamba
osati chifukwa cha kutalika kwa moyo
kapena kuchuluka kwa zaka,
9koma nzeru ndiye imvi za munthu,
moyo wosalakwa ndiye ukalamba wake.
10 Gen. 5.21-24; Mphu. 44.16; Ahe. 11.5 Panali munthu wina amene adaakomera Mulungu,
ndipo Mulungu adaamukonda.
Tsono pamene ankakhala pakati pa anthu ochimwa,
Mulungu adamtenga.
11Adamtengako kuti nsanje ingaipitse luntha lake,
chinyengo chingachimwitse mtima wake.
12Chifukwa kukopeka ndi zoipa kumadetsa m'maso,
zilakolako zamitundumitundu zimaipitsa
ngakhale mtima wolungama.
13Koma iyeyo pa nthaŵi yochepa
adasanduka wangwiro,
nakwaniritsa moyo wa zaka zambiri.
14Mtima wake udakomera Ambuye,
nchifukwa chake Ambuyewo adamuchotsa msanga
pakati pa zoipa.
15Anthu ankapenya zimenezi,
komabe sadazimvetse,
ndipo sadazisamale.
Sadazindikire kuti Mulungu amakomera mtima
osankhidwa ake,
ndi kuŵachitira chifundo,
ndikutinso amatchinjiriza anthu ake oyera mtima.
16Koma olungama amene afa
amatsutsa amene akali moyo
koma ali osamvera.
Ndipo anyamata oyera mtima otsirizika msanga
amatsutsa okalamba a zaka zambiri
pamene iwo ali osalungama.
17Anthu amaona kutha kwa munthu wolungama,
koma osamvetsa cholinga cha Chauta
chakuti imeneyi ndiye njira
yomutchinjirizira ku zoopsa.
18Anthu amamuwona nkumamunyoza,
koma Ambuye adzaŵanyodola iwowo.
Iwowo akadzafa, maliro ao adzakhala osalemekezeka,
adzanyozeka nthaŵi zonse
ngakhale pakati pa anthu akufa omwe.
19Ndithudi Ambuye adzaŵakantha
nkuŵagwetsa chadodolido,
iwowo pansi thi osanena kanthu.
Maziko ao adzagwedezeka,
anthu onsewo adzakhala ngati nthaka youma
yosabereka kanthu.
Adzamva mazunzo,
ndipo maina ao sadzakumbukikanso.
Za olungama ndi osalungama pa tsiku la chiweruzo20Pamene azidzaŵerengera machimo ao,
anthu ochimwawo adzabwera ali ndi nkhaŵa,
ndipo zoipa zaozo zidzaŵaukira nkuŵatsutsa.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.