Yer. 12 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Madandaulo a Yeremiya

1Inu Chauta nditati nditsutsane nanu,

wokhoza ndinu ndithu.

Komabe ndifuna kudandaulako kwa Inu

za mlandu wanga.

Chifukwa chiyani anthu oipa

zinthu zimaŵayendera bwino?

Chifukwa chiyani anthu osakhulupirika

amakhala pabwino?

2Inu mudaŵabzala, ndipo adamera mizu.

Amakula, namabala zipatso.

Amakonda kulankhula za Inu,

koma mitima yao ili kutali ndi Inu.

3Koma Inu Chauta ine mumandidziŵa.

Mumandiyang'ana, ndipo mumayesa mtima wanga,

nkuwona kuti ndimakukondani.

Muŵakoke anthu oipa ngati nkhosa zokaphedwa.

Muŵaike padera mpaka tsiku loti akaphedwe.

4Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti?

Ndipo udzu wake udzakhalabe wouma mpaka liti?

Palibe mbalame kapena nyama zimene zatsala

chifukwa anthu okhalamo ndi oipa kwambiri.

Amati, “Mulungu sadzaona zimene

zidzatiwonekere masiku athu otsiriza.”

5Chauta adayankha kuti,

“Ngati kukutopetsa kuthamanga ndi anthu,

nanga udzapikisana bwanji ndi akavalo?

Ngati mtima wako ulefuka m'dziko lokoma,

nanga udzatani m'nkhalango ya ku Yordani?

6Ngakhale abale ako ndi anansi ako

nawonso amakuchita chiwembu,

onsewo amvana pa zokuimba mlandu,

usaŵakhulupirire,

ngakhale alankhule nawe mau okoma.

Chauta aŵamvera chisoni anthu ake

7“Banja la Israele ndalisiya,

ndaŵataya anthu amene ndidaŵasankha.

Okondeka anga ndaŵapereka kwa adani ao.

8Anthu anga osankhidwa

asanduka ngati mikango yakuthengo,

amandidzumira mwaukali.

Nchifukwa chake ndimadana nawo.

9Anthu anga osankhidwa

ali ngati mbalame yamaŵangamaŵanga

imene akabaŵi aizinga kuchokera konsekonse.

Kasonkhanitseni nyama zakuthengo,

mubwere nazo ku phwando.

10Abusa ambiri adaononga munda wanga

wamphesa, adapondereza munda wanga.

Munda wokoma uja adausandutsa chipululu.

11Ndithu adausandutsa chipululu,

ukundilirira Ine uli wokhawokha.

Dziko lonse lasanduka chipululu,

ndipo palibe amene akusamalako.

12Anthu oononga abalalikira

ku zitunda zonse zam'chipululu.

Ndipo Ine Chauta ndatuma ankhondo kuti

akanthe dziko lonse,

kuyambira ku malire ena

mpaka ku malire enanso.

Palibe aliyense amene angapeze mtendere.

13Anthu adafesa tirigu,

koma adakolola minga.

Adadzitopetsa pogwira ntchito,

koma osapindula nkanthu komwe.

Zokolola zao nzochititsa manyazi,

chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Chauta.”

Za Chilango cha maiko ena

14Chauta akuti, “Anthu oipa onse oyandikana ndi Aisraele, akulanda Aisraelowo dziko, choloŵa chimene ndidapatsa anthu angawo. Nchifukwa chake ndidzaŵachotsa m'dziko limenelo, ndipo ndidzachotsa banja la Yuda pakati pao.

15Komabe nditaŵachotsa, ndidzaŵamveranso chifundo, ndipo ndidzabwezanso mtundu uliwonse ku dziko la choloŵa chake.

16Tsono iwo akadzaphunzira bwino njira za mayendedwe a anthu anga, ndi kumalumbira m'dzina langa kuti, ‘Pali Chauta Wamoyo,’ monga momwe iwo adaphunzitsira anthu anga kumalumbira m'dzina la Baala, ndiye kuti iwowo ndidzaŵakhazikitsa pakati pa anthu anga.

17Komatu ngati mtundu wina uliwonse sudzamvera Ine, ndidzauwononga kotheratu.”

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help