1Mwana wanga, munthu wosauka usamumane
zofunikira moyo wake,
kapena kumugwiritsa fuwa lamoto
munthu waumphaŵi.
2Usavute munthu wanjala,
kapena kumupsetsa mtima
munthu waumphaŵi.
3Munthu woŵaŵa mtima
usamuonjezere mavuto,
kapena kuchedwa kumuthandiza
pa zimene akupempha.
4Usamkanize munthu wovutika akakupempha,
kapena kufulatira munthu waumphaŵi.
5Usamapenya kumbali ukaona wosauka,
kapena kumpatsa zifukwa zoti akutemberere.
6Pakuti akakutemberera ali wovutika mu mtima,
Mlengi wake adzamva pemphero lakelo.
7Uzichita zoti anthu onse azikukonda,
ndipo uzilemekeza akuluakulu.
8Munthu wosauka akakulankhula,
umumvere,
akakupatsa moni,
uvomere mwamtendere ndi mofatsa.
9Ovutitsidwa uziŵapulumutsa kwa amene
akuŵavutitsa,
ndipo ukhale wolimba mtima pa kaweruzidwe kako.
10Kwa ana amasiye ukhale ngati bambo wao,
kwa mai wa anawo ukhale ngati mwamuna wake.
Pamenepo udzakhala ngati mwana wa Mulungu
Wopambanazonse,
ndipo Iye adzakukonda
koposa m'mene amakukondera mai wako.
Nzeru zili ngati mphunzitsi11Nzeru zimakweza ana ake
kuti akhale omveka,
zimasamala amene amazifunafuna.
12Amene amakonda nzeru,
amakonda moyo,
amene amazidzukirira m'mamaŵa
amapata chimwemwe.
13Munthu amene amakhala nazo,
anthu adzamlemekeza,
ndipo Ambuye adzamdalitsa
kulikonse kumene adzapite.
14Amene amatumikira nzeruzo,
amatumikiranso Woyera uja.
Ambuye amaŵakonda
amene amakonda nzeruzo.
15Munthu amene amatsata nzeru,
adzaweruza anthu a mitundu ina.
Amene amazimvera,
adzakhala ndi mtendere.
16Akazikhulupirira, adzakhala nazo,
ndipo zidzukulu zake zidzakhala nazonso.
17Poyamba zidzamuperekeza pa njira zokhotakhota,
ndi kumchititsa mantha ndi nthumanzi.
Zidzamuzunza pakumutsatitsa mwambo,
mpaka zidzamukhulupirire;
ndipo zidzamuyesa ndi malamulo ake.
18Pambuyo pake zidzabweranso kwa iye
ndi kumusangalatsa,
ndipo zidzamuululira zinsinsi zake.
19Koma akasokera, zidzamusiya,
zidzalola kuti aonongeke.
Za kuchita manyazi ndi kuwopa anthu20Uziyang'anira bwino
m'mene ziliri zonse,
ndipo uleke zoipa,
usati uzichita zokumvetsa manyazi.
21Pali manyazi ena ochimwitsa munthu,
pali manyazi enanso obweretsa ulemerero
ndi kuyanja.
22Usadzipweteke pakuchita zokondera,
usadzilakwitse pakuwopa anthu udyo.
23Usakhale chete pamene kulankhula
kukadakuthandiza,
usabise nzeru zako.
24Nzeru za munthu zimadziŵika nkulankhula kwake,
kuphunzira kwa munthu kumadziŵika ndi mau ake.
25Usamatsutsane ndi zoona,
uzikumbukira kuti ndiwe wosadziŵa zambiri.
26Usamachite manyazi kuvomera machimo ako,
usayese kukankhira m'mbuyo madzi a mtsinje.
27Usamagonjere chitsiru,
kapena kukondera anthu amphamvu.
28Uzilimbikira mpaka kufera zoona,
Ambuye adzakumenyera nkhondo.
29Usamalankhule mosaganizira bwino,
usamagwira mwamphwai ntchito zako.
30Usakhale woopsa ngati mkango m'nyumba mwako,
kapena kumazondazonda antchito ako.
31 Ntc. 20.35 Usatambalitse dzanja
kuti ulandire kanthu,
kapena kuliwumitsa
pa nthaŵi yobwezera zinthu.
Za kusadalira chumaWho We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.