Lun. 18 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kuyera kuŵalira Aisraele

1 Eks. 13.17-22 Koma kuyera kwakukulu kudaŵalira oyera anu.

Aejipito adamvadi mau ao,

ngakhale sadaone nkhope zao,

ndipo adaŵatcha odala,

popeza kuti analibe kanthu koŵavuta.

2Ndiye popeza kuti ana anuwo

sadalipsire pa mavuto ao,

Aejipito ankaŵathokoza

naŵapempha kuti aŵakhululukire

zolakwa zao zija.

3Tsono pamalo pa mdima,

Inu mudapatsa ana anu mtambo wamoto,

kuti uŵatsogolere pa njira yosaidziŵa iwowo.

Unali ngati dzuŵa losaŵavuta

pa ulendo wao wotchuka uja.

4Adani ao adayeneradi kuŵachotsera kuŵala

ndi kuŵatsekera mu mdima,

chifukwa adaaponya ana anu m'ndende.

Ana anuwo ndiwo amene anali odzapereka

kuŵala kwamuyaya kwa malamulo anu

kwa anthu a dziko lapansi.

Ana oyamba a ku Ejipito afa onse

5Iwo aja adafuna kupha ana a anthu anu oyera.

Koma mwana mmodzi uja ataikidwa

pa madzi a mtsinje nkupulumuka,

Inu mudaŵalanga anthuwo

pakupha ana ao ambirimbiri.

Ndipo mudaŵamiza onse pamodzi

m'mafunde aukali.

6Usiku umenewo makolo athu anali ataudziŵiratu,

kuti azilimba mtima ndi kukondwa

podziŵa kuti apherezera malumbiro

aja ankaŵakhulupiriraŵa.

7Choncho anthu anu

ankayembekeza chipulumutso cha olungama

ndiponso chiwonongeko cha adani ao.

8Njira yomwe mudalangira adani athu,

idakhala njira yoti mutichitire ife zaulemu

potiitana kwa Inu.

9Adzukulu oyera mtima a olungama aja

ankapereka nsembe mobisala.

Ankavomerezana kuti adzasunga malamulo a Mulungu

ndi kugaŵana molingana zinthu zimodzimodzi,

kaya zikhale madalitso, kaya zoopsa.

Motero adaayambiziratu kuimba nyimbo zotamanda

za makolo ao.

10Koma nthaŵi yomweyo konsekonse kudamveka mfuu

wosokonezeka wa adani ao akulira ana ao.

11Kapolo ndi mbuye wake adalandira chilango chimodzi,

munthu wamba adavutika chimodzimodzi monga mfumu.

12Onsewo anali ndi maliro osaŵerengeka

a amene adafa imfa imodzimodzi.

Sipadatsale amoyo okwanira oti nkuika maliro onsewo,

chifukwa ana ao amene iwo ankanyadira kwambiri

adafa kamodzinkamodzi.

13Adakana kukhulupirira chilichonse

chifukwa cha masenga ao,

koma pamene adafa ana ao oyamba,

anthuwo adazindikira

kuti mtundu wa anthu anu

unalidi wa ana a Mulungu.

14Pamene zinthu zonse zinali chete,

ndipo usiku utafika pakati pake,

15mau anu amphamvu adalumpha

kuchokera kumwamba ku mpando wachifumu,

kudzagwa m'dziko lotembereredwa

ngati wankhondo wopanda chisoni.

16Wokhala ndi lupanga lakuthwa

la lamulo lanu losasinthika,

adaima ndi kudzaza dziko ndi imfa,

mapazi ake ataponda pansi,

mutu wake utakhudza ku thambo.

17Pompo maloto oopsa adaŵachititsa mantha,

zinthu zozilota ndi zoziwona m'masomphenya zidaŵaopsa.

18Atagwa pansi, wina uku, wina uku,

nkukhala ngati akufa,

aliyense adaulula zifukwa zake zimene ankafera.

19Maloto aja amene adaŵavuta

anali ataŵadziŵitsiratu zimenezo,

kuwopa kuti angafe osazindikira chifukwa chake

cha mazunzo ao.

Pemphero la Aroni lipulumutsa Aisraele ku imfa

20 Num. 16.41-50 Ngakhalenso anthu olungama omwe, imfayo idaŵakhudza,

ndipo m'chipululu muja mliri udagwetsa ambiri.

Koma mkwiyo wanu sudakhalitse nthaŵi yaitali.

21Munthu wina wosapalamula adafulumira

kuŵatchinjiriza,

ndipo atatenga zida za utumiki wake,

adapemphera ndi kufukiza lubani wopepesera machimo.

Motero adaletsa ukali wanu, nathetsa mliri uja,

kuwonetsa kuti analidi mtumiki wanu.

22Adaletsa ukali wanuwo,

osati chifukwa cha nyonga za thupi,

kapena chifukwa cha mphamvu za zida,

koma adafeŵetsa mtima wa wolangayo ndi mau ake,

pomukumbutsa malumbiro ake

ndiponso zimene adaapangana ndi makolo athu.

23Akufa aja atagwa ndi kuunjikika pa mulu umodzi,

iye adanenera anthu naletsa ukali wanu,

ndipo adautsekera njira kuti amoyo usaŵagwere.

24Pamkanjo pake panali chithunzi

cha dziko lonse lapansi,

maina olemekezeka a makolo athu anali olembedwa

pa mizere inai ya miyala ya mtengo wapatali.

Tsono ulemerero wanu unkaoneka

pa chisoti cha pamutu pake.

25Poona zimenezo, woononga uja adaima,

ankachita nazo mantha,

chifukwa kunkakwanira kuwonetsa

chitsanzo cha ukali wanu.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help