Yes. 9 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Mt. 4.15 Koma anthu amene anali ndi nkhaŵa, sadzakhalanso otaya mtima. Masiku amakedzana Mulungu adaanyozetsa dziko la Zebuloni ndi la Nafutali, koma kutsogolo kuno adzalisandutsa laulemu dera lonseli, kuyambira ku nyanja yaikulu kuzambwe mpaka kukafika ku dziko la patsidya pa mtsinje wa Yordani, ndiye kuti dziko la Galilea, dziko la anthu a mitundu ina.

Aneneratu za mfumu yam'tsogolo

2 Mt. 4.16; Lk. 1.79 Anthu amene ankayenda mumdima

aona kuŵala kwakukulu.

Amene ankakhala m'dziko la mdima wandiweyani,

kuŵala kwaŵaonekera.

3Inu Chauta, mwauchulukitsa mtundu wanu,

mwaonjezera kukondwa kwa anthu anu.

Iwo akukondwa pamaso panu

monga m'mene anthu amakondwera nthaŵi ya masika,

monganso m'mene anthu amakondwera pogaŵana zofunkha.

4Pakuti inu mwathyola goli limene linkaŵalemera,

ndodo zimene ankamenyera mapewa ao,

ndiponso mikwapulo ya anthu oŵazunza,

monga mudaachitira pogonjetsa Amidiyani.

5Ndithu, nsapato iliyonse ya munthu wankhondo

ndi chovala chilichonse chothonyezekera magazi,

zidzatenthedwa pa moto ngati nkhuni.

6Chifukwa mwana watibadwira,

mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife.

Ulamuliro udzakhala m'manja mwake,

ndipo adzamtchula dzina lake lakuti

“Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu,

Atate Amuyaya, Mfumu ya Mtendere.”

7 Lk. 1.32, 33 Ulamuliro ndi mtendere wake zidzanka zikukulirakulira.

Iye adzakhala pa mpando wa mfumu Davide,

ndipo adzakhazikitsa ndi kuchirikiza ufumu wake,

pochita zachilungamo ndi zangwiro

kuyambira nthaŵi imeneyo mpaka muyaya.

Ndi mtima wake wonse Chauta Wamphamvuzonse

watsimikiza kuti adzachitadi zimenezi.

Achenjeza Aisraele kuti adzalangidwa

8Ambuye atumiza mau otsutsa Yakobe,

mauwo agwa pa Aisraele, zidzukulu zake.

9Anthu onse, ndiye kuti Aefuremu

ndi anthu okhala m'Samariya,

adzazimva zotsatira zake za mau ameneŵa.

Iwo amalankhula monyada ndi modzikuza kuti,

10“Ngakhale njerwa zagumuka,

ife tidzamanga ndi miyala yosema.

Ngakhale mitanda yamkuyu yagwetsedwa,

ife tidzaika mitanda yamkungudza m'malo mwake.”

11Koma Chauta waŵautsira adani,

Waŵakhwirizira adaniwo kuti amenyane nawo.

12Asiriya chakuvuma ndi Afilisti

chakuzambwe ayasama kukamwa kuti adye Aisraele.

Komabe mkwiyo wa Mulungu sudaŵachoke

chifukwa cha zonsezi,

ndipo mkono wake uli chisamulirecho

kufuna kuŵalanga.

13Anthuwo sadabwerere kwa Mulungu

amene adaŵakantha uja,

sadalape ndi kufunafuna Chauta Wamphamvuzonse.

14Nchifukwa chake Chauta wadula

mutu wa Israele pamodzi ndi mchira womwe,

nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe

pa tsiku limodzi.

15Mutuwo ukutanthauza akuluakulu ndi olemekezeka,

mchirawo ukutanthauza aneneri

ophunzitsa zabodza.

16Pakuti amene amatsogolera anthuŵa amaŵasokeza,

ndipo otsogoleredwawo amatayika.

17Nchifukwa chake Ambuye sadzakondwera nawo achinyamata,

ndipo sadzaŵachitira chifundo

ana amasiye ndi akazi amasiye.

Pakuti aliyense ndi wosasamala za Mulungu

ndiponso ndi wochimwa.

Pakamwa paliponse pamalankhula zopusa.

Komabe mkwiyo wa Mulungu sudaŵachoke

chifukwa cha zonsezi,

ndipo mkono wake uli chisamulirecho

kufuna kuŵalanga.

18Kuipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto,

moto wake wotentha mkandankhuku ndi minga.

Umayatsanso nkhalango

ndipo utsi wake umachita kuti toloo

ngati mtambo wochindikira.

19Nchifukwa chake mkwiyo wa Chauta

Wamphamvuzonse watentha dziko,

ndipo anthu ali ngati nkhuni zosonkhera moto.

Palibe munthu wochitira chifundo mbale wake.

20Ku dzanja lamanja amapeza ndi kudya

chakudya, koma osakhuta,

ku dzanja lamanzere amapeza ndi kudya

chakudya, koma njala ali nayobe.

Kwatsala nkumangodyana okhaokha.

21Amanase akuthira Aefuremu nkhondo,

Aefuremu akuthira Amanase nkhondo.

Onsewo pamodzi akumenyana ndi Yuda.

Komabe mkwiyo wa Mulungu sudaŵachoke

chifukwa cha zonsezi,

ndipo mkono wake uli chisamulirecho

kufuna kuŵalanga.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help