Yes. 35 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chimwemwe cha Yerusalemu m'tsogolo

1Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala,

dziko louma lidzakondwa ndi kuchita maluŵa.

2Dzikolo lidzakhala ndi maluŵa ochuluka

ongodzimerera okha.

Lidzasangalala ndi kufuula ndi chimwemwe.

Lidzakhala ndi ulemerero wonga wa mapiri a ku Lebanoni,

maonekedwe ake adzakhala okongola

ngati a ku Karimele ndi Saroni.

Aliyense adzaona ulemerero wa Chauta

ndi ukulu wa Mulungu wathu.

3 Ahe. 12.12 Mulimbitse manja ofooka,

ndi kuŵapatsa mphamvu maondo olobodoka.

4Muuze onse a mtima wamantha kuti,

“Limbani mtima, musachite mantha.

Mulungu wanu akubwera kudzalipsira ndi kulanga adani anu.

Akubwera kudzakupulumutsani.”

5 Mt. 11.5; Lk. 7.22 Pamenepo maso a anthu akhungu adzaphenyuka,

ndipo makutu a agonthi adzatsekuka.

6Opunduka adzalumpha ngati mphoyo,

ndipo osalankhula adzaimba mokondwa.

Akasupe adzatumphuka m'chipululu,

ndipo mitsinje idzayenda m'dziko louma.

7Mchenga wotentha udzasanduka nyanja,

ndipo dziko louma lidzasanduka la akasupe.

Pamene panali mbuto za nkhandwe

padzamera udzu ndi bango.

8Kumeneko kudzakhala mseu waukulu

wotchedwa “Mseu Wopatulika.”

Ochimwa sadzayendamo,

ndipo zitsilu sizidzasokera m'menemo.

9Kumeneko sikudzakhala mikango,

ndipo nyama zoopsa sizidzafikako,

sizidzapezeka konse kumeneko.

Koma okhawo amene Chauta

adaŵapulumutsa,

adzayenda mu mseu umenewu.

10Amene Chauta adaŵaombola adzabwerera,

ndipo adzafika ku Ziyoni akuimba mosangalala.

Kumeneko adzakondwa mpaka muyaya,

ndipo adzaona chimwemwe ndi chisangalalo.

Chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help