Bar. 5 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Yes. 52.1; 61.3, 10; Chiv. 21.2 Iwe Yerusalemu, vula chovala chako chamaliro

ndi chachisoni.

Uvale mpaka muyaya zovala za ulemerero wa Mulungu.

2Funda mwinjiro wachilungamo

wochokera kwa Mulungu.

Vala chisoti cha ulemerero wa Mulungu wamuyaya.

3Chifukwa Mulungu akufuna kuŵonetsa ulemerero wako

kwa onse okhala pansi pa thambo lakumwamba.

4Mulungu adzakutcha dzina

limene mpaka muyaya lidzakhala

“Mtendere wa chilungamo,”

ndipo “Ulemerero wa chipembedzo.”

5Dzuka, iwe Yerusalemu,

imirira pamtundapo,

uyang'ane kuvuma.

Ona ana ako amene Woyera uja waŵasonkhanitsa

kuyambira kuvuma mpaka kuzambwe.

Akukondwa pakuti Mulungu waŵakumbukira.

6Adakusiya akuyenda pansi,

adani ao ataŵatenga.

Koma Mulungu adzaŵabwezanso kwa iwe,

ataŵanyamula mwaulemerero

ngati ana a ku nyumba ya mfumu.

7Pajatu Mulungu adalamula

kuti mapiri aatali ndi zitunda zosatha azichepetse,

ndiponso kuti zigwa azifotsere

kuti mbali zonse zilingane.

Motero Aisraele adzayenda mwamtendere

mu ulemerero wa Mulungu.

8Potsata lamulo la Mulungu

nkhalango ndi mitengo yonse ya fungo labwino

zidzaŵakonzera mthunzi Aisraele.

9Zoonadi Mulungu adzatsogolera Aisraele mwachimwemwe

ndi kuŵala kwa ulemerero wake,

ndiponso ndi chifundo ndi chilungamo chake.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help