1 Mphu. 24.23 Nzeru ndiye buku la Malamulo a Mulungu.
Malamulo ake odzakhala mpaka muyaya.
Onse ozigwiritsa nzeruzo, amakhala ndi moyo,
koma olekana nazo amafa.
2Bwerera Yakobe, udzalandire nzeru,
yenda molondola kuŵala kwa kuyera kwake.
3Ulemerero wako usapatse munthu wina,
madalitso ako usaŵapereke kwa anthu achilendo.
4Inu Aisraele, ifetu ndife odala,
chifukwa timadziŵa zokomera Mulungu.
Yerusalemu alimbikitsa chikhulupiriro cha ana ake5Limbani mtima, anthu anga,
inu amene mumamveketsa dzina la Israele.
6Adakugulitsani kwa anthu akunja,
koma osati kuti muwonongekeretu.
Mudakwiyitsa Mulungu,
nkuwona adakuperekani kwa adani anu.
7Mudamputadi Mlengi wanu
popereka nsembe ku mafano,
m'malo mozipereka kwa Mulungu.
8Mudaiŵala Mulungu wamuyaya
amene adakulerani.
Mudamvetsa chisoni Yerusalemu
amene anali ngati mai wanu.
9Iye adaona ukali wa Mulungu ukukugwerani,
ndipo adati,
“Mvetserani, inu anthu okhala pafupi ndi Ziyoni,
Mulungu wanditumizira mavuto aakulu.
10“Ndidaonerera ana anga aamuna ndi aakazi
akutengedwa kupita nawo kuukapolo
kumene Mulungu wamuyaya adaŵatumiza.
11Ndinkaŵalera ndi chimwemwe,
koma poŵaona akutengedwa ukapolo,
ndidamva chisoni ndi kulira misozi.
12Ndiye wina aliyense asakondwerere mavuto angaŵa,
pamene tsopano ndili wamasiye,
ndipo ana anga ambiri adandisiya.
Ndidakhala choncho ndekhandekha
chifukwa cha machimo a ana angawo,
popeza kuti iwowo adasiya malamulo a Mulungu.
13Sadalabadeko nkomwe za malamulo ake,
sadatsate konse njira za malamulo ake,
sadalole kuti Mulungu aŵaongolere
m'njira ya chilungamo.
14“Tsono bwerani kuno,
inu anthu okhala pafupi ndi Ziyoni!
Kumbukirani ukapolo wa ana anga aamuna ndi aakazi
ku dziko lachilendo
kumene Mulungu wamuyaya adaŵatumizako moŵalanga.
15Paja Mulungu adaŵadzetsera
mtundu wa anthu akutali,
kuti udzaŵathire nkhondo,
mtundu wopanda manyazi,
wolankhula chilankhulo chosadziŵika,
mtundu wosalemekeza anthu okalamba,
mtundu wosamvera chifundo ndi ana omwe.
16Anthu a mtundu umenewu
adatenga ana aamuna okondedwa a mai wamasiye,
adalanda ana aakazi a mai wotsala yekha,
kumusiya nalira.
17“Nanga ine ndingakuthandizeni bwanji?
18Pajatu amene adakugwetserani mavuto ameneŵa
ndi iyeyo amene angakupulumutseni kwa adani anu.
19 2Es. 2.2 Pitani ana anga, inde pitani!
Ine ndatsala ndekha.
20Ndavula mkanjo wa masiku amtendere,
ndavala chiguduli chamaliro.
Ndidzalira kwa Mulungu wanga wamuyaya
pa moyo wanga wonse.
21“Limbani mtima, ana anga,
pempherani kwa Mulungu.
Iye adzakupulumutsani ku mavuto
ndiponso kwa adani anu.
22Inetu ndikukhulupirira
kuti Mulungu wamuyaya adzakupulumutsani.
Woyera uja wandisangalatsa
chifukwa cha chifundo
chimene chidzakufikireni posachedwapa
kuchokera kwa Mpulumutsi wanu wamuyaya.
23Ndidakuwonererani mukupita kutali
muli ndi chisoni mu mtima ndi misozi m'maso.
Koma Mulungu adzakubwezaninso kwa ine
muli ndi chimwemwe ndi chisangalalo,
kuti mukhale nane mpaka muyaya.
24Anthu okhala pafupi ndi Ziyoni amene
adakuwonani mukutengedwa ukapolo,
posachedwa adzaona Mulungu akukupulumutsani.
Chipulumutsocho chidzakufikirani
ndi ulemerero waukulu
ndiponso ndi ukulu wodabwitsa wa Mulungu wamuyaya.
25Ana anga, pirirani mosaŵinya
mkwiyo wa Mulungu umene udakugwerani.
Adani anu adakusautsani,
koma posachedwa mudzaŵaona akuwonongeka,
mudzaŵaponda pa khosi ndi mapazi anu.
26Ana anga okondedwa adayenda m'njira zokhakhala,
ndipo adaŵatenga ngati gulu la zoŵeta
zimene mdani wazifunkha.
27“Limbani mtima, ana anga,
pempherani kwa Mulungu,
chifukwa amene adakulangani chotereyo,
yemweyonso adzakukumbukirani.
28Monga mwa kufuna kwanu mudasiyana ndi Mulungu,
momwemonso mutembenukire kwa Iye,
mumufunefune ndi mtima wanu wonse.
29Pakuti monga momwe Iye adakugwetserani m'mavuto,
momwemonso adzakupulumutsani,
ndipo mudzakhala osangalala mpaka muyaya.”
Asangalatsa Yerusalemu30Limba mtima, iwe Yerusalemu.
Amene adakutcha dzina uja,
yemweyonso adzakusangalatsa.
31Anthu amene adakuchita zoipa,
nkukondwerera kuwonongeka kwako,
adzapeza mavuto.
32Kumizinda kumene ana ako adakazunzikirako ukapolo,
kudzaoneka mavuto.
Mavutonso adzagwera mzinda
umene udalandira ana ako ngati akaidi.
33Pakuti monga momwe mzindawo udakondwerera
kugwa kwako,
nkusangalala chifukwa cha kuwonongeka kwako,
momwemonso mzindawo udzavutika
pamene uwo womwewo udzapasuka.
34Ndidzauchotsera chimwemwe
chonyadira kuchuluka kwa anthu ake,
chikondwerero chake chidzasanduka maliro.
35Moto wochokera kwa Mulungu wamuyaya
udzatentha mzindawo pa masiku ambiri,
ndipo kumeneko kudzakhala ademoni
pa nthaŵi yaitali.
36Yang'ana kuvuma, iwe Yerusalemu,
ona chimwemwe chimene Mulungu akukutumizira.
37Ona alikudza ana ako,
amene udaŵaonerera akupita ku dziko lachilendo.
Alikudzadi,
Woyera uja ataŵasonkhanitsa
kuchokera kuvuma mpaka kuzambwe,
akukondwerera ulemerero wa Mulungu.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.