Yes. 18 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kudzalangidwa kwa Etiopiya

1 Zef. 2.12 Tsoka kwa anthu okhala ku dziko la

patsidya pa mitsinje ya Etiopiya!

Kumeneko kumamveka mkokomo wa mapiko.

2Kuchokera ku dzikolo amatuma akazembe

pa mtsinje wa Nailo m'mabwato agumbwa

omangoyandama pa madzi.

Tsono pitani inu amithenga aliŵiro

kwa mtundu wa anthu ataliatali

ndi a khungu losalala,

oopedwa ndi anthu akufupi ndi akutali omwe,

mtundu wamphamvu ndi wogonjetsa mitundu ina,

anthu amene dziko lao nlodukanadukana ndi mitsinje.

3Inu nonse anthu a pa dziko lapansi,

inu amene mumakhala pansi pano,

pamene mbendera yakwezedwa pa mapiri,

muyang'ane!

Lipenga likamalira, mumve!

4Pakuti Chauta adandiwuza kuti,

“Kumene ndili Ineko,

ndidzangoyang'ana pansi mwakachetechete,

monga m'mene dzuŵa limaŵalira nthaŵi yotentha,

monganso m'mene amagwera mame usiku

pa nthaŵi yakholola.”

5Anthu asanayambe kukolola, maluŵa

atayoyoka ndipo mphesa zitayamba kupsa,

Iye adzadula mphukira ndi chigwandali,

ndipo adzasadza nthambi zotambalala.

6Mitembo ya ankhondowo adzasiyira

mbalame zam'mapiri zodya nyama,

ndiponso zilombo zakuthengo.

Mbalame zidzaidya pa nthaŵi ya chilimwe,

ndipo zilombo zakuthengo

zidzaidya pa nthaŵi ya chisanu.

7Pa nthaŵi imeneyo

anthu adzabwera ndi zopereka

kwa Chauta Wamphamvuzonse.

Anthu ake adzakhala aatali ndi a khungu losalala,

oopedwa ndi anthu akufupi ndi akutali omwe,

mtundu wamphamvu ndi wogonjetsa mitundu ina,

anthu amene dziko lao ndi lodukanadukana ndi mitsinje.

Zoperekazo adzabwera nazo ku phiri la Ziyoni

kumene anthu amapembedza Chauta Wamphamvuzonse.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help