Lun. 9 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pemphero la Solomoni lopempha luntha

1 1Maf. 3.6-9; Lun. 7.7 “Mulungu wa makolo anga, Ambuye achifundo

ndinu amene mudalenga zinthu zonse ndi mau anu.

2Ndi nzeru zanu mudalenga munthu,

kuti azilamulira zolengedwa zonse

zimene Inu mudazipanga,

3kuti aweruze dziko lino lapansi

ndi mtima wangwiro ndi wolungama,

ndipo kuti azigamula milandu mosakondera.

4Mundipatse luntha limene limakhala

pafupi ndi mpando wanu wachifumu,

musandichotse m'gulu la ana anu.

5Ndinedi mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu.

Ndine munthu wofooka ndi wa moyo wochepa.

Ndimangomvetsa pang'ono za chilungamo ndi malamulo.

6Ngakhale munthu akhale wangwiro

pakati pa ana a anthu,

koma popanda luntha lochokera kwa Inu,

anthu adzamuyesa wopanda pake.

7“Ndinu mudandisankhula

kuti ndikhale mfumu ya anthu anu,

ndi kumaweruza ana anu aamuna ndi aakazi.

8Mudandilamula kuti ndikumangireni Nyumba

pa phiri lanu loyera,

ndiponso guwa lansembe

mu mzinda umene Inu mumakhalamo,

potsata chitsanzo cha chihema choyera

chimene mudachikonza poyamba paja.

9Luntha limakhala nanu,

ndipo limadziŵa ntchito zanu.

Linali nanu pamene munkalenga dziko lapansi.

Limadziŵa zimene zili zabwino pamaso panu,

ndi zimene zili zolungama

potsatana ndi malamulo anu.

10Mulitumize kuchokera ku dziko loyera lakumwamba

ndi ku mpando wanu waulemerero,

kuti likhale nane ndi kundithandiza pa ntchito zanga,

ndipo lindidziŵitse zokomera Inu.

11Luntha limadziŵa ndi kumvetsa zonse.

Lidzanditsogolera mochenjera pa ntchito zanga

ndipo lidzanditchinjiriza ndi ulemerero wake.

12Tsono ntchito zanga zidzakhala zovomerezeka,

ndidzaweruza anthu anu molungama,

ndipo ndidzakhala woyenerera

mpando waufumu wa atate anga.

13“Kodi ndani angathe kudziŵa maganizo a Mulungu?

Ndani angathe kuzindikira zimene Ambuye akufuna?

14Nzeru za anthu nzopereŵera,

zolinga zathu nzotha kulephera.

15Chifukwa thupi lodzafali limalemetsa mtima,

nyumba yake yadothiyi imavuta mtima woganiza zambiri.

16Nkwapatali kale kwa ife

kulota zimene zili pansi pano,

ndipo timachita kuvutikira kuti timvetse

ngakhale zimene zili pafupi nafe.

Nanji tsono zimene zili kumwamba,

angazitulukire ndani?

17Ndani angathe kudziŵa kufuna kwanu Ambuye,

mutapanda kumupatsa luntha,

kapena kumutumizira mzimu wanu woyera

kuchokera kumwamba?

18Motero njira za anthu a pansi pano

zidalungamitsidwa,

anthu adaphunzira zimene zimakukomerani,

ndipo adapulumuka chifukwa cha luntha.”

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help