Lun. 16 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Nyama zosautsa Aejipito zithandiza Aisraele

1Aejipito adalangidwa ndi zolengedwa zotere

monga kudaŵayenera,

adazunzikadi ndi zilombo zosaŵerengeka.

2 Eks. 16.11-13; Num. 11.31, 32 M'malo mwa chilangocho, mtundu wa anthu anu

mudauchitira chifundo.

Ndipo pofuna kuthetsa nkhuli yao,

mudaŵakonzera zinziri, chakudya chokoma.

3Aejipito aja, ngakhale ankafuna kudya,

ataona tizilombo toŵazunza,

adanyansidwa ndi zakudya zofunika zomwe,

koma anthu anu atamva njala nthaŵi pang'ono,

pambuyo pake adalandirako chakudya chokoma.

4Kunali koyenera kuti njala yaikulu

isautse anthu aja ovuta mtundu wanu,

koma anthu anu mudafuna kuti apenye chabe

mavuto ogwera adani aowo.

Mliri wa dzombe ndi njoka

5 Num. 21.6-9 Pamene anthu anu ankasauka ndi ukali wa zilombo

ndipo pamene ankafa, njoka zaululu zitaŵaluma,

mkwiyo wanu sudapitirire.

6Iwo adavutika nthaŵi pang'ono ngati chenjezo chabe,

ndipo adalandira pomwepo chizindikiro

cha chipulumutso, choŵakumbutsa malamulo anu.

7Aliyense amene ankatembenukira chizindikirocho, ankapulumuka.

Sindikuti chimene adachiwonacho

ndicho chidaŵapulumutsa,

koma ndi Inuyo amene muli mpulumutsi wa anthu onse.

8Pakutero mudaonetsa adani athu aja

kuti ndinu amene mumapulumutsa ku zoipa zonse.

9Iwowo adafa chifukwa choŵaluma dzombe ndi nchenche,

osapeza mankhwala opulumutsira moyo wao,

chifukwa anali oyenera kulangidwa choncho.

10Koma ana anu, ngakhale mano a njoka zaululu

sadathe kuŵatsiriza,

chifukwa chifundo chanu

chidzaŵathandiza ndi kuŵachiritsa.

11Adalumidwa kuti azikumbukira mau anu,

mudaŵachiritsa msanga, kuti angakuiŵaleni

ndipo angapande kulandira chithandizo chanu.

12Si masamba, si mankhwala adaŵachiritsa,

koma ndi mau anu, Inu Ambuye,

amene amachiza matenda onse.

13Inu muli ndi mphamvu pa moyo ndi pa imfa,

mumafikitsa anthu ku khomo la imfa,

ndi kuŵabweza kuchokera kumeneko.

14Munthu amene ali woipa mtima

angathe kupha munthu mnzake,

koma sangathe kubweza mpweya utachoka,

kapena kupulumutsa mzimu

utaloŵa m'dziko la akufa.

Matalala ndi Mana

15Kuthaŵa dzanja lanu nkosatheka.

16Anthu osamvera, okana kukudziŵani,

adakwapulidwa ndi mphamvu za dzanja lanu.

Mvula yamkuntho ndi yamatalala,

ndiponso mvumbi wosakata, zidaŵasautsa,

ndipo moto udaŵatentha.

17Chinali chinthu chozizwitsa

kuti moto udayaka mwamphamvu

ngakhale m'madzi momwe mozimitsa zonse,

chifukwa zonse zapansipano

zimachirikiza anthu olungama.

18Mwina ukali wa moto unkacheperapo

kuti usapsereze tizilombo todzasautsa osamverawo,

kuti motero adaniwo poona zimenezo,

azizindikira chiweruzo cha Mulungu choŵalondola.

19Mwina moto unkayaka kwambiri

ngakhale m'madzi momwe,

kuti uwononge dzinthu dzonse

dza dziko la anthu osamvera.

20 Eks. 16.1-36 Pamalo pa zimenezi mudadyetsa anthu anu

ndi chakudya cha angelo,

mudaŵatumizira buledi wokonzeka kale

wofumira kumwamba,

popanda iwo kugwirapo ntchito.

Chinali chakudya chosangalatsa

ndi chokomera anthu onse,

ngakhale a kukonda kosiyanasiyana.

21Chakudya chanucho

chinkasonyeza kukoma mtima kwanu kosamalira ana anu.

Chinali chokomera aliyense,

ndipo kukoma kwake kunkasinthika

malinga nkukonda kwa munthu aliyense.

22Chipale ndi chisanu choundana chambee

sizidasungunuke m'moto,

kuti anthu anu azindikire kuti unali moto

woyaka pakati pa matalala

ndi pakati pa mvula,

umene unkaononga dzinthu dza adani ao.

23Koma moto womwewo unkaiŵala khalidwe lake,

kuti olungama zakudya zao zisaonongeke.

24Zoonadi, zolengedwa, potumikira Inu Mlengi wake,

zimalimbikira kuti zilange anthu oipa,

koma zimakhululuka ndi kuŵachitira zachifundo

anthu okhulupirira Inu.

25Choncho, nthaŵi yakaleyo,

potenga maonekedwe osiyanasiyana,

zolengedwazo zinkathandiza ufulu wanu wolera onse,

potsata khumbo la anthu okupemphani.

26Tsono ana anu amene mumaŵakonda, Inu Ambuye,

adatha kuphunzira kuti si zokolola zokha

zimene zingadyetse anthu,

koma ndi mau anu amene amasunga anthu okukhulupirirani.

27Zimene sizidaonongeke ndi moto,

zidasungunuka ndi chitungu cha pakanthaŵi,

cha mwendo umodzi wa dzuŵa.

28Choncho tidziŵe kuti

tiyenera kudzuka ndi kukuyamikani,

dzuŵa lisanatuluke,

ndipo tiyenera kupemphera kwa Inu

nthaŵi yomwe ya mbandakucha.

29Koma munthu wosathokoza, chikhulupiriro chake

chidzasungunuka ngati chipale,

ndi kutayika ngati madzi opanda ntchito.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help