Mas. 77 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kusangalala pa nthaŵi yamavutoKwa Woimbitsa Nyimbo. Kutsata maimbidwe a Yedutuni. Salmo la Asafu.

1Ndikulira mopemba kwa Mulungu,

ndi mau okweza ndikufuula kwa Mulungu kuti andimve.

2Pa tsiku lamavuto ndimafunafuna Ambuye.

Usiku wonse ndimakweza manja anga

ndi kupemphera kosalekeza.

Mtima wanga umakana kuusangalatsa.

3Ndikamalingalira za Mulungu,

ndimangobuula mumtima.

Ndikamasinkhasinkha za Iye,

ndimataya mtima.

4Mumagwira zikope zanga kuti ndisagone tulo.

Ndikuvutika kwambiri

kotero kuti sindingathe kulankhula.

5Ndimalingalira za masiku akale,

ndimakumbukira zaka zamakedzana.

6Ndimasinkhasinkha mumtima mwanga usiku.

Ndimadzifunsa ndi kufufuzafufuza mumtima mwanga.

7Ndimati,

“Kodi Ambuye adzandikana mpaka liti?

Kodi sadzandikomeranso mtima?

8Kodi chikondi chao chosasinthika chija chatheratu?

Kodi malonjezo ao aja atha mpaka muyaya?

9Kodi Mulungu waiŵala kukoma mtima kwake kuja?

Kodi wakwiya ndi kuleka chifundo chake chija?”

10“Chondiŵaŵa ndi chakuti,

Mulungu Wopambanazonse wasintha mchitidwe wake.”

11Komabe ndidzakumbukira ntchito zanu, Inu Chauta,

inde, ndidzakumbukira zodabwitsa zanu zakalekale.

12Ndidzasinkhasinkha za zonse zimene mwachita,

ndidzalingalira za ntchito zanu zamphamvuzo.

13Njira zanu, Inu Mulungu, nzoyera.

Kodi alipo mulungu winanso wamkulu ngati Mulungu wathu?

14Inu ndinu Mulungu amene mumachita zodabwitsa,

amene mwaonetsa mphamvu zanu pakati pa mitundu ya anthu.

15Mudaombola anthu anu ndi mkono wanu wamphamvu,

ndiye kuti ana a Yakobe ndi Yosefe.

16Pamene madzi adakuwonani, Inu Mulungu,

pamene madzi adakuwonani, adachita mantha,

inde, nyanja yakuya idanjenjemera.

17Mitambo idachucha madzi,

mumlengalenga mudachita bingu.

Zing'aning'ani mbali ndi mbali.

18Phokoso la bingu lanu lidamveka konsekonse,

mphezi zanu zidaŵalitsa dziko lonse,

dziko lapansi lidanjenjemera ndi kugwedezeka.

19Inu mudadzera pa nyanja,

njira yanu idadzera pa madzi akuya,

komabe mapazi anu sadaoneke.

20Mudatsogolera anthu anu ngati nkhosa

kudzera mwa Mose ndi Aroni.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help