Yes. 32 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mfumu yachilungamo

1Nthaŵi ina kudzakhala mfumu ina

yolamulira mwaungwiro,

ndiponso nduna zina zoweruza mwachilungamo.

2Aliyense mwa iwo adzakhala ngati

pothaŵirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe.

Adzakhala ngati mitsinje yoyenda m'dziko louma,

ndipo ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu m'chipululu.

3Maso a anthu openya sadzakhalanso otseka,

ndipo makutu a anthu akumva adzakhala otchera.

4Anthu a mtima waphamphu

adzadziŵa kuchita zinthu moganiza bwino,

ndipo anthu achibwibwi

adzalankhula mosadodoma ndi momveka.

5Chitsiru sichidzalandira ulemu,

ndipo munthu woipa sadzalemekezeka.

6Munthu wopusa amalankhula zauchitsilu,

ndipo amaganiza kuchita zoipa.

Amachita zoipira Mulungu,

amalankhula zonyoza Mulungu.

Anjala saŵapatsa chakudya,

aludzu saŵapatsa chakumwa.

7Munthu wachabechabe njira zake nzoipa.

Amalingalira zaupandu kuti aŵachite chiwembu

anthu osauka pakuŵanamizira,

ngakhale pamene osaukawo ali osalakwa konse.

8Koma munthu wa mtima wabwino

amalingalira zabwino,

ndipo amalimbikira kuchita zabwino.

Chenjezo kwa akazi osasamala

9Tatiyeni, inu akazi aulesi, mumve mau anga.

Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikulankhula.

10Pakapita chaka ndi masiku pang'ono,

mudzanjenjemera inu akazi amatama,

chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika,

zipatsonso sizidzaoneka.

11Dederani inu akazi aulesi,

njenjemerani, inu odzikhulupirira udyo.

Vulani zovala, ndipo muvale nsanza m'chiwuno.

12Dzimenyeni pa chifuŵa mwachisoni,

chifukwa minda yachonde ndi yamphesa yaonongeka,

13ndipo minga ndi mkandankhuku

zikumera pa dziko la anthu anga.

Ndithu, mulire nyumba zonse

zimene ankakhalamo mosangalala,

ndiponso mzinda umene udaali ndi chimwemwe.

14Nyumba yaufumu idzasiyidwa,

ndipo mzinda wonse udzakhala wopanda anthu.

Malinga ake ndi nsanja yomwe

zidzasanduka mapanga mpaka muyaya.

Abulu akuthengo adzasangalala kumeneko,

ndipo ziŵeto zidzapeza busa komweko.

15Koma Mulungu adzatitumizira mzimu wake,

kuchokera kumwamba,

ndipo dziko lachipululu lidzasanduka lachonde,

minda yonse idzabereka dzinthu dzambiri.

16Pamenepo m'dziko lonse mudzakhala chilungamo,

kuyambira ku chipululu mpaka ku minda yachonde.

17Chifukwa anthu onse akamachita zachilungamo,

m'dziko mudzakhala mtendere ndi bata mpaka muyaya.

18Anthu a Mulungu adzakhala m'midzi yamtendere,

m'nyumba zokhulupirika, ndiponso m'malo ousira abata.

19Komabe nkhalango idzaonongedwa ndi matalala,

ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi.

20Anthu adzakondwa kwambiri

chifukwa adzakhala ndi madzi ambiri,

ndipo abulu ndi ng'ombe zao azidzadya paliponse.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help