Mla. 1 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Zapansipano nzothetsa nzeru

1Naŵa mau a Mlaliki, mwana wa Davide,

mfumu ya ku Yerusalemu:

2Zonse nzopanda phindu, akutero Mlaliki.

Zonse nzachabechabe!

Ndithudi zonse nzopandapake.

3Kodi munthu amapindulanji

ndi ntchito zonse zolemetsa

zimene amazigwira pansi pano?

4 Mphu. 14.18 Mbadwo wina ukutha, wina ukudza,

koma dziko lapansi limakhalapobe losasinthika.

5Dzuŵa limatuluka, nkukaloŵa,

ndipo limapita mwamsanga kumene linatulukira.

6Mphepo imaombera chakumwera,

nkudzakhotera chakumpoto.

Imaomba mozungulirazungulira,

pozungulirapo nkudzabwereranso komwe yachokera.

7Mitsinje yonse imakathira ku nyanja,

koma nyanjayo osadzaza.

Kumene madzi adachokera

amabwereranso komweko.

8Zinthu zonse nzolemetsa,

kulemera kwake nkosasimbika.

Maso sakhuta nkupenya,

makutunso sakhuta nkumva.

9Zomwe zidaalipo kale

ndizo zidzakhaleponso.

Zomwe zidaachitika kale

ndizo zidzachitikenso.

Ndiye kuti chatsopano palibiretu pansi pano.

10Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti,

“Ichi ndiye nchatsopano?”

Iyai, chidaalipo kale,

ifenso kukadalibe nkomwe.

11Zakale sizikumbukika,

ngakhale zinthu zimene zidzachitike pambuyo pake

sizidzakumbukikanso

ndi amene adzabwere m'tsogolo mwake.

Nzeru nzodzetsa chisoni

12Ine Mlalikine ndidakhalapo mfumu yolamulira Israele ku Yerusalemu.

13Ndidaaika mtima wanga pa kufunitsitsa kumvetsa bwino zonse zochitika pansi pano. Imeneyi ndi ntchito yolemetsa kwambiri imene Mulungu adatipatsa anthufe.

14Zonse zochitika pansi pano ndaziwona. Zonsezo nzopandapake, ndipo kuzifunafuna nkungodzivuta chabe.

15Chimene chidakhota sichingathe kuwongokanso,

chimene palibe sichingathe kuŵerengedwa.

16 1Maf. 4.29-31; Mphu. 47.14-18 Mumtima mwangamu ndinkati, “Ndatola nzeru zambiri, kupambana onse amene ankalamulira ku Yerusalemu kale. Ndaphunzira zambiri zaluntha ndi zanzeru.”

17Ndidaayesetsa kumvetsa kuti nzeru nchiyani, misala nchiyani, uchitsiru nchiyani. Koma ndidazindikira kuti kuterokonso kunali kungodzivuta chabe.

18Paja nzeru zambiri zimadzetsa chisoni chambiri,

munthu akamaonjezera nzeru,

ndiye kuti akuwonjezeranso chisoni.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help