Mas. 8 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Za ulemerero wa Mulungu ndi wa munthuKwa Woimbitsa Nyimbo. Kutsata maimbidwe a Gititi.Salmo la Davide.

1Chauta, Ambuye athu,

dzina lanu ndi lotchuka pa dziko lonse lapansi.

Kumwamba amaimba nyimbo zotamanda ulemerero wanu.

2 Mt. 21.16 Nawonso ana ndi makanda omwe amauimbira.

Mwamanga linga chifukwa cha adani anu,

kuti mugonjetse onse okuukirani.

3Ndikamayang'ana ku thambo lanu

limene mudapanga ndi manja anu,

ndikamaona mwezi ndi nyenyezi

zimene mudazikhazika kumeneko,

4 Yob. 7.17, 18; Mas. 144.3; Ahe. 2.6-8 ndimadzifunsa kuti,

“Kodi munthu nchiyani

kuti muzimkumbukira,

mwana wa munthu nchiyani

kuti muzimsamalira?”

5 Lun. 2.23; Mphu. 17.1-4 Ndiyetu mudamlenga mochepera pang'ono

kwa Mulungu amene,

mudampatsa ulemerero ndi ulemu wachifumu.

6 1Ako. 15.27; Aef. 1.22; Ahe. 2.8 Mudampatsa ulamuliro pa ntchito za manja anu.

Mudamgonjetsera zolengedwa zonse,

7nkhosa, ng'ombe ndi nyama zakuthengo,

8mbalame zamumlengalenga, nsomba zam'nyanja,

ndi zonse zoyenda pansi pa nyanja.

9Chauta, Ambuye athu,

dzina lanu ndi lotchuka pa dziko lonse lapansi.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help