1Chauta akunena kuti,
“Ndidzautsa mphepo yoti idzaononge Babiloni
pamodzi ndi onse okhala m'dziko la Babiloni.
2Ndidzatuma alendo ku Babiloni,
kuti adzampepete ndi kuseseratu zonse
zokhala m'dziko lake.
Iwowo adzamuukira pa mbali zonse nthaŵi ya zoopsayo.
3Okoka uta musaŵalekerere,
kapena onyadira chovala chao chankhondo.
Anyamata ake musasiyeko ndi mmodzi yemwe.
Ankhondo ake onse muŵaononge.
4Adzavulazidwa ndi kufera m'dziko lonse
ndi m'miseu ya mzinda wao womwe.
5Israele ndi Yuda sadasiyidwe ndi Mulungu wao,
Chauta Wamphamvuzonse.
Koma dziko la Ababiloni nlodzaza ndi machimo,
machimo ake onyoza Woyera uja wa Israele.
6“Aliyense mwa inu athaŵe, achoke ku
Babiloni kuti apulumutse moyo wake.
Musaphedwe naye pamodzi
pamene adzalandira chilango chake.
Limeneli ndilodi tsiku limene Chauta adzaŵalanga,
ndipo adzaŵalipsira kwathunthu.
7 Chiv. 17.2-4; 18.3 Pajatu Babiloni anali ngati chikho
chagolide m'manja mwa Chauta,
kuti aledzeretse dziko lonse lapansi.
Mitundu yambiri ya anthu idamwako vinyo wake,
nchifukwa chake idapenga.
8Babiloni wagwa mwadzidzidzi ndipo waonongeka.
Mlireni, mfunireni mankhwala,
kuti mwina nkuchira.
9 Chiv. 18.5 Ena adati, ‘Tidayesa kumpatsa mankhwala koma sadachire.
Tiyeni tingomsiya, timchokere
ndipo aliyense apite ku dziko lakwao.
Paja mlandu wake wafika mpaka kumwamba,
wafika mpaka ku mlengalenga.’ ”
10Tsono Chauta waonetsa poyera
kuti ifeyo ndife osalakwa.
Tiyeni tilengeze ku Ziyoni
zimene Chauta, Mulungu wathu, watichitira.
11“Songolani mivi,
tengani zishango.”
Chauta wautsa mitima ya mafumu a Amedi, poti cholinga chake nchoti aononge Babiloni. Afuna kumlipsira chifukwa choononga Nyumba yake.
12Kwezani mbendera yankhondo
ndipo muwononge malinga a Babiloni.
Mulimbitse oteteza, muike alonda,
mukonzekere kulalira.
Pakuti Chauta watsimikiza,
ndipo adzachitadi zimene adanena za anthu a ku Babiloni.
13 Chiv. 17.1 Inu amene muli ndi mitsinje yambiri,
ndinu olemera kwambiri,
koma chimalizo chanu chafika,
moyo wanu watha.
14Chauta Wamphamvuzonse adalumbira pali
Iye yemwe mwini wake kuti,
“Ndidzatuma anthu osaŵerengeka ngati dzombe
kuti adzakuthireni nkhondo,
ndipo adzafuula,
kuwonetsa kuti apambana.”
Nyimbo yotamanda Mulungu15Chauta ndiye amene adalenga dziko lapansi
ndi mphamvu zake.
Ndiye amene adapanga zonse ndi nzeru zake,
ndipo ndi umisiri wake adayala thambo lakumwamba.
16Iye akalankhula, kumamveka mkokomo wa madzi kumwamba,
ndiye amene amadzetsa mitambo
kuchokera ku malekezero a dziko lapansi.
Amang'animitsa mphezi za mvula,
amakunthitsa mphepo kuchokera kumene amaisunga.
17Anthu onse ndi opusa, alibe nzeru.
Mmisiri aliyense wosula amachita manyazi
ndi mafano ake.
Mafano amene amapangawo ngabodza,
mwa iwo mulibe konse moyo.
18Mafanowo ngachabechabe, oyenera kuŵaseka,
ndipo pamene anthuwo adzalangidwe,
mafanowo adzaonongedwa.
19Koma Mulungu wa Yakobe sali ngati mafanowo,
Iye ndiyedi Mlengi wa zonse.
Aisraele ndi anthu ake amene Iye adaŵasankha,
dzina lake ndi Chauta Wamphamvuzonse.
20Iwe Babiloni ndiwe nyundo yanga,
chida changa chankhondo:
ndi iwe ndimaphwanyaphwanya mitundu ya anthu,
ndimaononga maufumu.
21Ndi iwe ndimaphwanyaphwanya akavalo
ndi okwerapo ao.
Ndi iwe ndimaphwanyaphwanya magaleta
ndi oyendetsa ake.
22Ndi iwe ndimaphwanyaphwanya amuna ndi akazi ao.
Ndi iwe ndimaphwanyaphwanya nkhalamba ndi achinyamata.
Ndi iwe ndimaphwanyaphwanya anyamata ndi anamwali.
23Ndi iwe ndimaphwanyaphwanya abusa ndi ziŵeto zao.
Ndi iwe ndimaphwanyaphwanya alimi ndi ng'ombe zao.
Ndi iwe ndimaphwanyaphwanya abwanamkubwa
ndi atsogoleri ankhondo.
Za chilango cha Babiloni24“Inu mukupenya, ndidzalipsira Babiloni ndi onse okhalamo chifukwa cha zolakwa zonse zimene adachita ku Ziyoni,” akutero Chauta.
25“Ndikukuimba mlandu, iwe phiri loononga,
iwe amene umasakaza dziko lonse lapansi.
Ndidzasamula dzanja langa pofuna kukulanga,
ndi kukugubuduzira kunsi kuchokera pa mathanthwe ako.
Ndidzakusandutsa phiri lopserera.
26Palibe mwala wako ndi umodzi womwe umene
adzabwere nawo kuti augwiritse ntchito ngati
mwala wapangodya.
Iwe udzakhala chipululu mpaka muyaya,”
akutero Chauta.
27“Kwezani mbendera yankhondo pa dziko,
lizani lipenga kuti mitundu ya anthu imve.
Itanani mitundu yonse kuti imuthire nkhondo Babiloni.
Itanani maufumu a ku Ararati,
a ku Mini ndi a ku Asikenazi.
Ikani mtsogoleri wankhondo kuti amenyane
ndi Babiloniyo.
Mubweretse akavalo ochuluka ngati dzombe.
28Sonkhanitsani mitundu ya anthu kuti imuthire nkhondo.
Muitane mafumu a ku Medi, pamodzi ndi
abwanamkubwa ndi nduna zao,
ndiponso ankhondo a m'maiko onse amene amaŵalamulira.
29Dziko likunjenjemera,
likuphiriphitha chifukwa cha kupweteka,
chifukwa zimene Chauta adakonzera Babiloni
zidzachitikadi,
zakuti adzamsandutsa dziko lachipululu
lopanda anthu.
30Ankhondo a ku Babiloni aleka kuponya nkhondo,
angokhala khale m'malinga ao.
Mphamvu zao zatha,
asanduka ngati akazi.
Nyumba zake zatenthedwa,
mipiringidzo ya zipata zake yathyoka.
31Othamanga akungopezanapezana,
amithenganso akungotsatanatsatana.
Onsewo akukauza mfumu ya ku Babiloni
kuti mbali zonse za mzinda wake zalandidwa.
32Madooko onse alandidwa,
malo obisalako alonda atenthedwa,
ndipo ankhondo ake onse asokonezeka.
33Babiloni wokongola uja wangokhala ngati popunthira
tirigu pa nthaŵi yopuntha kumene.
Ndipotu posachedwa nthaŵi yake yokolola ifika,”
akutero Chauta Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israele.
34A ku Yerusalemu akuti,
“Nebukadinezara mfumu ya ku Babiloni, watiwononga,
Watitswanya ndi kutitaya ngati mbiya yopanda kanthu.
Watimeza ngati ng'ona.
Wakhuta ndi zakudya zathu zotsekemera,
kenaka nkutilavula.”
35Anthu okhala m'Ziyoni anene kuti,
“Zankhanza zimene Ababiloni
adatichita ife ndi ana athu ziŵabwerere.”
Anthu okhala mu Yerusalemu anene kuti,
“Magazi athu amene adamwazika
aŵagwere Ababiloniwo ngati chilango chao.”
Zakuti Chauta adzathandiza Aisraele36Nchifukwa chake Chauta akunena kuti,
“Ndidzakumenyera nkhondo yako,
ndipo ndidzakulipsirira.
Ndidzaumitsa nyanja ya ku Babiloni,
akasupe ake onse adzaphwa.
37Motero Babiloni adzasanduka mulu wa nyumba zopasuka,
malo a nkhandwe, malo oopsa ndi onyozeka,
opanda wina wokhalamo.
38“Ababiloni adzakhuluma ngati mikango.
Adzadzuma ngati ana a mikango.
39Akachita dyera, ndidzaŵakonzera madyerero.
Tsono ndidzaŵaledzeretsa,
ndipo adzasangalala nkugona tulo tampakampaka,
osadzukanso ai.
40Ndidzapita nawo kuti akaphedwe ngati anaankhosa,
ngati nkhosa zamphongo kapena atonde,”
akutero Chauta.
Za tsoka la Babiloni41“Ndithu Babiloni wagonjetsedwa,
mzinda umene dziko lonse lapansi
linkaunyadira walandidwa.
Ogo! Babiloni uja wasanduka chinthu
chonyansa pakati pa mitundu ya anthu!
42Nyanja yakwera mpaka kumiza Babiloni,
waphimbidwa ndi mafunde ake.
43Mizinda yake yasanduka malo onyansa,
dziko louma ndi lachipululu,
dziko lopanda anthu losayendako mwanawamunthu.
44Ndidzalanga Beli, mulungu wa Ababiloni,
ndidzamsanzitsa zimene adameza.
Mitundu ya anthu sidzapitanso kwa iye.
Malinga a Babiloni agwa!
45Tulukani m'Babiloni, inu anthu anga!
Fulumirani, pulumutsani moyo wanu!
Thaŵani mkwiyo woopsa wa Chauta!
46Musataye mtima.
Musaope maphephe amene awanda m'dziko monse.
Chaka ndi chaka pamabuka ndithu maphephe
onena za nkhondo pa dziko lapansi,
ndiponso zakuti mfumu yakutiyakuti
ikumenyana ndi inzake.
47“Tsono ikudza nthaŵi
pamene ndidzalange mafano a Babiloni.
Dziko lonselo lidzachita manyazi.
Anthu ake onse ophedwa adzakhala ali
ngundangunda pakati pake.
48 Chiv. 18.20 Pambuyo pake dziko lakumwamba ndi dziko
lapansi ndi zonse zokhala m'menemo zidzaimba
mokondwera chifukwa cha kugwa kwa Babiloni.
Anthu oononga ochokera kumpoto adzamgonjetsa,”
akutero Chauta.
49 Chiv. 18.24 Babiloni ayeneradi kugwa chifukwa cha amene
adaphedwa ku Israele,
monga adagwera anthu a pa dziko lonse lapansi
amene adaphedwa ndi iyeyo.
Uthenga wa Chauta kwa Aisraele ku Babiloni50“Inu amene mwapulumuka ku nkhondo ya Babiloni,
chokanipo apa, musazengereze.
Kumbukirani Chauta ngakhale muli kutali ndi kwanu,
muzimkumbukira Yerusalemu.
51Inu mukuti ‘Tikuchita manyazi
chifukwa cha manyozo amene talandira.
Nkhope zathu zagwa
chifukwa anthu achilendo aloŵa ku mabwalo
opatulika a ku Nyumba ya Chauta.’ ”
52Koma Chauta akunena kuti,
“Ikubwera nthaŵi
pamene ndidzalange mafano a ku Babiloni,
ndipo kubuula kwa anthu olasidwa
kudzamveka m'dziko lake lonse.
53Ngakhale Babiloni adzikweze mpaka ku mlengalenga,
nkulimbitsa nsanja zake,
ndidzatuma oononga kuti amgonjetse,”
akutero Chauta.
Kuwonongeka kwa Babiloni kunkirankira54“Imvani mau olira m'Babiloni.
Imvani phokoso la kuwonongeka kwakukulu
m'dziko la Ababiloni.
55Ndithu, Chauta akuwononga Babiloni,
ndipo akuthetsa phokoso lake lalikulu.
Mfuu wa anthu ake ukumveka ngati mafunde amkokomo,
phokoso lake likukwererakwerera.
56Woononga amufikira Babiloni,
ndipo ankhondo ake onse agwidwa,
mauta ao athyoka.
Pajatu Chauta ndi Mulungu wolanga,
adzabwezeradi kwathunthu zoipa zao.
57Ndidzaledzeretsa akuluakulu ake pamodzi
ndi anzeru ake.
Ndidzaledzeretsa abwanamkubwa ake, atsogoleri
ankhondo, ndi ankhondo ake amene.
Adzagona tulo tampakampaka, tosadzuka nato,”
ikutero mfumu imene dzina lake ndi Chauta Wamphamvuzonse.
58Chauta Wamphamvuzonse akunena kuti,
“Malinga aakulu a Babiloni adzasalazidwa.
Zipata zake zazitali zidzatenthedwa.
Mitundu ya anthu idagwira ntchito pachabe,
anthu adangotopa nkumanga zimene tsopano
zikupsa ndi moto.”
Yeremiya atumiza uthenga ku Babiloni59Mfumu Zedekiya anali ndi phungu wake wamkulu, dzina lake Seraya, mwana wa Neriya, mdzukulu wa Maseiya. Pa chaka chachinai cha ufumu wa Zedekiya ku Yuda, Seraya adatsagana ndi mfumuyo kupita ku Babiloni. Tsono mneneri Yeremiya adampatsirako uthenga Serayayo.
60Yeremiya anali atalemba m'buku za chiwonongeko chonse cha Babiloni, ndiponso za zina zonse zokhudza Babiloni.
61Yeremiyayo adauza Seraya kuti, “Pamene ukafike ku Babiloni, usakalephere kuŵaŵerengera anthu mau onseŵa.
62Ukanene kuti, ‘Inu Chauta, mwalengeza cholinga chanu chofuna kuwononga malo ano, osasiyapo kanthu, munthu kapena nyama. Ndipo adzakhala chipululu mpaka muyaya.’
63Chiv. 18.21 Ukakatha kuŵerenga bukulo, ukalimangire ku mwala, nkuliponya mu mtsinje wa Yufurate.
64Ndipo ukanene kuti, ‘Umu ndimo m'mene Babiloni adzamirire. Sadzadzukanso chifukwa cha zoopsa zonse zimene ndidzamgwetsere.’ ” Mau a Yeremiya athera pamenepa.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.