Yes. 53 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Aro. 10.16; Yoh. 12.38 “Ndani wazikhulupirira zimene tamvazi?

Ndani wazindikira mphamvu za Chauta pa zimenezi?

2Pajatu mtumiki wake uja adakula

ngati chiphukira pamaso pa Mulungu,

ndiponso ngati muzu m'nthaka youma.

Iye analibe maonekedwe enieni

kapena nkhope yabwino,

kuti ife nkumamuyang'ana.

Analibe kukongola koti ife nkukokeka naye.

3Iye uja anthu adamnyoza ndipo adamkana.

Anali munthu wamasautso, wozoloŵera zoŵaŵa.

Anali ngati munthu amene anzake

amaphimba kumaso akamuwona.

Anthu adamnyoza, ndipo ife sitidamuyese kanthu.

4 Mt. 8.17 “Ndithudi, iye adapirira masautso

amene tikadayenera kuŵamva ifeyo,

ndipo adalandira zoŵaŵa

zimene tikadayenera kuzilandira ifeyo.

Koma ife tinkaganiza kuti

ndi Mulungu amene akumlanga,

ndi kumkantha ndi kumsautsa.

5 1Pet. 2.24 Koma adambaya chifukwa cha machimo athu,

ndipo adamtswanya chifukwa cha zoipa zathu.

Chilango chimene chidamgwera iye

chatipatsa ife mtendere,

ndipo mabala ake atichiritsa.

6 1Pet. 2.25 Tonse tidaasokera ngati nkhosa.

Aliyense mwa ife ankangodziyendera.

Ndipo Chauta adamsenzetsa iyeyo machimo athu.

7 Chiv. 5.6 Ntc. 8.32, 33 “Anthu adamsautsa ndi kumzunza,

koma iye sadalankhule kanthu.

Monga momwe amachitira mwanawankhosa

wopita naye kuti akamuphe,

ndiponso monga momwe nkhosa imakhalira duu poimeta,

nayenso adangokhala chete.

8Adamgwira mwankhanza namuzenga mlandu,

ndipo adapita naye kukamupha.

Mwa anthu anzake ndani adalabadako

zoti iye adachotsedwa m'dziko la anthu amoyo?

Ndani adalabadako kuti iye uja

adalangidwa chifukwa cha machimo a anthu?

9 1Pet. 2.22 Adamkonzera manda ake pakati pa manda a achifwamba.

Adamuika m'manda pakati pa anthu olemera,

ngakhale iye sadachitepo chosalungama

chilichonse ndipo

sadanene bodza lililonse.”

10Komabe ndi Chauta yemwe

amene adaafuna kuti amuzunze,

ndipo adamsautsadi.

Iye adapereka moyo wake

kuti ukhale nsembe yokhululukira machimo.

Choncho adzaona zidzukulu zake,

adzakhala ndi moyo wautali,

ndipo chifuniro cha Chauta chidzachitika mwa iye.

11Atatha mazunzo akewo,

adzaona phindu lake, ndipo adzakhutira.

Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo

adzasenza machimo a anthu onse

kuti iwo ambiri a iwo asadzapezekenso kuti ndiopalamula.

12 Mk. 15.28; Lk. 22.37 Motero Ine ndidzampatsa ulemu woyenerera akuluakulu.

Adzagaŵana zofunkha ndi ankhondo amphamvu,

popeza kuti adapereka moyo wake mpaka kufa,

ndipo adamuyesa mnzao wa anthu ophwanya malamulo.

Adasenza machimo a anthu ambiri,

ndipo adaŵapempherera ochimwawo kuti akhululukidwe.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help