1Chidakwa sichilemera, ngakhale chikhale pa ntchito.
Munthu wonyoza zinthu zazing'ono, amanka naagwa
pang'onopang'ono.
2Zoledzeretsa ndiponso akazi zimaononga anthu anzeru.
Munthu wokonda akazi adama amatha manyazi moipa.
3Potsiriza pake adzakhala chakudya cha mphutsi ndi
nyongolotsi,
kupanda manyazi kwakeko kudzamuphetsa.
Kulankhula zachabe nkoipa4Kukhulupirira munthu msanga kumaonetsa mtima
wosaganiza bwino,
ndipo kuchimwa kumapweteka wochimwa yemweyo.
5Munthu wokondwerera machimo
adzalangidwa.
6Koma wodana ndi ukazitape
zoipa zimamuchepera.
7Usamabwerezabwereza zimene udamva,
ndipo sudzapeza mavuto.
8Kaya ndi bwenzi wako kaya ndi mdani wako,
usamkambire,
usaulule pokhapokha ngati nkuchimwa kukhala chete.
9Mwina ena nkumva mau akowo nayamba kusakukhulupirira,
pambuyo pake nkudzadana nawe.
10Ngati wamva mphekesera, zithere mwa iwe.
Usachite mantha, sungaphulike nazo.
11Chitsiru chikamva kanthu, chimamva kupweteka mu mtima
ngati kupweteka kwa mkazi pobala mwana.
12Mumtima mwa chitsiru mukaloŵa nkhani,
ndiye ngati mpaliro wazika m'ntchafu.
Usakhulupirire zonse zakumva13Umfunse bwenzi wako, mwina mwake sadachite kanthu,
ndipo ngati adachita kanthu,
ndiye kuti sadzachitanso.
14Umfunse mnzako, mwina mwake sadanene kanthu.
Ngati adanenadi, sadzanenanso.
15Umfunse bwenzi lako, poti osinjirira ngambiri.
Usakhulupirire zonse zokuuza anthu.
16Mwina munthu amalankhula padera mosafuna.
Kodi ndani asanachimwe konse polankhula.
17Usanaopseze mnzako, uyambe wamufunsa bwino,
uleke Malamulo a Mulungu Wopambanazonse agwire ntchito.
18Kuwopa Ambuye ndiye chiyambi choti atikomere mtima,
ngati uli ndi luntha Ambuye amakukonda.
19Kudziŵa Malamulo a Ambuye ndiye mwambo wopatsa moyo.
Amene amachita zokomera Ambuye, amadya za mtengo wa moyo wosatha.
Za nzeru zoona ndi zonyenga20Nzeru nkuwopa Ambuye,
nzeru nkutsata Malamulo ndi kudziŵa kuti Mulungu
ndiye Wamphamvuzonse.
21Wantchito wouza mbuye wake kuti, “Sindichita
zimene mukufuna,”
ngakhale pambuyo pake achitebe,
zimamupsetsa mtima munthu womsunga uja.
22Komatu kukhala wodziŵa pa zoipa si nzeru,
malangizo a anthu ochimwa sangakuphunzitse zanzeru.
23Pali kuchenjera kwina kumene anthu amadana nako
ndipo pali zitsiru zina zongokhala zopanda nzeru.
24Ndi bwino kukhala woopa Mulungu uli wopanda nzeru
kupambana kukhala ndi nzeru zambiri uli wophwanya Malamulo.
25Pali kuchenjera kwina kwenikweni ndithu koma
kosalungama,
palinso anthu opotoza zoona kuti zinthu ziŵayendere bwino.
26Pali tambwali woyenda ŵeraŵera kuwonetsa chisoni,
pamene mumtima mwake ali wonyenga.
27Amaphimba nkhope namadziwonetsa ngati wosamva,
koma ngati palibe wina woyang'ana, amakuchenjerera.
28Pali ena amene sachimwa chifukwa chosoŵa mphamvu,
koma akangopeza danga, amachita ndithu zoipa.
29Munthu ungathe kumdziŵira maonekedwe,
ndipo munthu wanzeru amazindikirika
ndi pamaso pomwe.
30Zovala za munthu ndi kasekedwe kake
ndiponso kayendedwe,
zonsezi zimaonetsa mkhalidwe wake.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.