Mphu. 46 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Yoswa

1 Yos. 1.1—11.23 Yoswa, mwana wa Nuni, anali ngwazi yankhondo,

ndiye amene adaloŵa m'malo mwa Mose pa ntchito

ya uneneri.

Potsata tanthauzo la dzina lake,

adasanduka wotchuka pa ntchito yopulumutsa

osankhidwa a Ambuye.

Adagonjetsa adani amene ankaŵathira nkhondo,

ndi kupatsa Aisraele dziko laolao.

2Anthu ankachita chidwi poona m'mene ankakwezera manja ake,

ndi m'mene ankasamulira lupanga lake

pochita nkhondo ndi mizinda.

3Nkale lonse ndani adaonetsa kulimba mtima ngati kwa iyeyu?

Pajatu ndiye amene ankamenya nkhondo za Ambuye.

4Kodi suja adaaimitsa dzuŵa

mpaka tsiku limodzi lidaatalika ngati masiku aŵiri?

5Adapemphera Mphambe Wopambanazonse

pamene adani ankampanikiza ku mbali zonse,

ndipo Ambuye amphamvu adayankha pemphero lake

pogwetsa matalala oopsa.

6Adakantha anthu a dzikolo

ndipo adaonongeratu adani ake pa Matsitso paja,

kuti mitundu ya anthu adziŵe mphamvu ya zida zake,

poti iye ankamenyera nkhondo Ambuye,

ndipo ankamvera Wamphamvu uja kotheratu.

Kalebe

7 Num. 14.6-10; 11.21; Yos. 14.6-11 Pa nthaŵi ya Mose, Yoswa uja ndi Kalebe, mwana wa Yefune,

adakhala okhulupirika polimbana ndi gulu lonse.

Adaletsa anthu kuti angachimwe

nathetsa kudandaula kwao.

8Mwa anthu oyenda pansi 600,000 aŵiri

okhawo ndiwo adapulumuka,

nakaloŵa m'dziko laolao, dziko lamwanaalirenji.

9Ambuye adampatsa nyonga Kalebe,

ndipo iye adakhala nazo mpaka nthaŵi ya

ukalamba wake.

Adakwera m'dziko lamapiri,

nalilanda kuti likhale la zidzukulu zake.

10Tsono Aisraele onse adaona

kuti ndi chinthu chabwino kutsata Ambuye mokhulupirika.

Aweruzi

11 Owe. 1.1—16.31 Panalinso aweruzi, aliyense wotchuka pa yekha.

Onsewo adakana kupembedza mafano,

ndipo sadapandukire Ambuye.

Aŵakumbukire moŵalemekeza.

12Mafupa ao apeze moyo watsopano

kuchokera kumanda kumene akugona,

ndipo mbiri ya kutchuka kwao ibukenso mwa adzukulu ao.

Samuele

13 1Sam. 3.19, 20; 7.9-11; 10.1; 12.3; 16.13; 28.18, 19 Ambuye adakonda kwambiri Samuele.

Ali mneneri wa Ambuye, adakhazikitsa ufumu,

ndipo adadzoza olamulira anthu ake.

14Nthaŵi zonse adaweruza anthu potsata

Malamulo a Ambuye,

ndipo Ambuyewo adasunga bwino Yakobe.

15Poti Samuele adakhala wokhulupirika,

adaoneka kuti anali mneneri weniweni.

Pa mau ake anthu adazindikira kuti analidi

mneneri woona.

16Adapemphera Ambuye Amphamvuzonse,

pamene adani ankampanikiza ku mbali zonse,

ndipo adapereka nsembe ya mwanawankhosa.

17Pamenepo mau a Ambuye adagunda kumwamba

ngati bingu,

adamveka ndi phokoso lalikulu.

18Adaononga atsogoleri a adani

ndiponso atsogoleri onse a Afilisti.

19Samuele asanakapumule kwamuyaya,

adachita umboni pamaso pa Ambuye ndi pa

wodzozedwa wake kuti,

“Sindidatengepo chinthu cha munthu wina,

ngakhale nsapato,”

ndipo palibe amene adamtsutsa.

20Ngakhale atafa, adalosabe

nachenjeza mfumu Saulo za imfa yake.

Ali m'manda adalankhula mau olosa

kuti machimo a anthu ake afafanizike.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help