Hos. 10 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1Aisraele ali ngati mpesa wokondwa

umene unkabala zipatso zambiri.

Chuma chao chikamanka chichuluka,

chipembedzo chachikunja chinkakulirakuliranso.

Dziko lao likamanka litukuka,

iwo ankakometserakometsera mafano ao

amene ankaŵapembedza.

2Mtima wao ndi wonyenga.

Tsopano ayenera kulangidwa chifukwa cha machimo ao.

Chauta adzagumula maguwa ao ansembe,

ndipo adzaononga miyala yao yoimiritsa yachipembedzo.

3Posachedwa anthuwo adzanena kuti,

“Tilibe mfumu tsopano chifukwa sitidamvere Chauta.

Komabe mfumuyo ikadatichitira chiyani ife?”

4Mafumu akungolankhula mau opandapake.

Amangochita zipangano ndi malonjezo abodza.

Chilungamo chasanduka kusalungama

kumene kumaphuka ngati udzu woipa m'munda.

5Anthu a ku Samariya adzachita mantha,

fano la mwanawang'ombe la ku Betehaveni

likadzaonongedwa.

Anthu ake adzalirira.

Nawonso ansembe ake aja adzalira maliro a mulungu waoyo,

chifukwa ulemerero wake wonse wachokeratu.

6Zoonadi, fanolo lidzatengedwa kupita ku Asiriya,

kuti likakhale mphatso yoperekedwa kwa mfumu yaikulu.

Aefuremu adzachita manyazi,

Aisraelewo adzachita manyazi

chifukwa cha malangizo onama amene ankamvera.

7Mfumu ya ku Samariya idzatengedwa kunka kutali

ngati kanthambi koyenda pa madzi.

8 Lk. 23.30; Chiv. 6.16 Akachisi opembedzerako milungu yabodza

amene Aisraele ankachimwirako,

idzaonongedwa.

Minga ndi mitungwi zidzamera pa maguwawo.

Anthu adzauza mapiri kuti, “Tigwereni!”

Adzauza magomo kuti, “Tipsinjeni!”

Aisraele adzagonjetsedwa pa nkhondo

9 Owe. 19.1-30 Chauta akuti,

“Kuyambira uchimo wa ku Gibea,

Aisraele akhala akuchimwabe.

Motero adzagonjetsedwa pa nkhondo ku Gibea komweko.

10Ndidzabwera kudzalimbana ndi anthu aupanduŵa

kuti ndiŵalange.

Anthu a mitundu ina adzasonkhana kuti aŵathire nkhondo

chifukwa cha uchimo wao waukulu.

11Kale Efuremu anali ngati ng'ombe yophunzitsidwa

imene inkakonda kupuntha tirigu.

Tsopano m'khosi lake lokongola ndaikamo goli,

kuti agwire ntchito koposa.

Ndifuna kuti Yuda azitipula,

Yakobe azimwanya mauma.

12 Yer. 4.3 Mudzifesere m'chilungamo,

ndipo mudzakolola madalitso

a chikondi changa chosasinthika.

Tipulani tsala lanu

pakuti nthaŵi yofunafuna Chauta yakwana.

Funafunani Chautayo

mpaka atabwera kudzakugwetserani mvula ya madalitso.

13Mudabzala zolakwa,

ndipo mudakolola chilango chake.

Mwadya zotsatira zake za mabodza.

Chifukwa choti mwadalira magaleta anu,

ndi kuchuluka kwa anthu anu a nkhondo,

14adani anu adzakuthirani nkhondo.

Malinga anu onse adzaonongedwa

monga momwe Salamani adaonongera Betaribele

pa tsiku la nkhondo.

Adaphwanya azimai pamodzi ndi ana omwe.

15Momwemo zidzakuchitikirani inu a ku Betele

chifukwa cha uchimo wanu waukulu.

Nkhondo ikadzangoyamba m'mamaŵa,

nayonso mfumu ya ku Israele idzaphedwa.”

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help