Nyi. 1 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 1Maf. 4.32 Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.

Nyimbo Yoyamba

Mkazi

2Undimpsompsone ndi milomo yako,

chifukwa chikondi chako nchoposa vinyo kukoma kwake.

3Mafuta ako odzola ngonunkhira bwino,

dzina lako likundikumbutsa za mafuta otsanyukako.

Nchifukwa chaketu, atsikana sangaleke kukukonda.

4Tenge, ndizikutsata, tiye tifulumire.

Iwe mfumu yanga, kandiloŵetse m'chipinda mwako.

Tizisangalala kwambiri ndi kukondwa limodzi.

Chikondi chako tichitamande kupambana vinyo.

Akazi onse amakukondera kaone!

5Inu akazi a ku Yerusalemu,

ine ndine wakuda inde,

komatu wokongola tsono.

Ndine wakuda ngati mahema a ku Kedara,

komabe wokongola ngati makatani

a m'nyumba ya Solomoni.

6Musandiyang'ane monyoza

chifukwa cha kudaku,

ndi dzuŵatu lidandidetsali.

Alongo anga adandikwiyira,

mpaka kukandigwiritsa ntchito m'minda yamphesa.

Koma munda wangawanga, osatha kuusamala.

7Tandiwuza, iwe wokondedwa wanga wapamtima,

kumene umadyetsa ziŵeto zako,

kumene umazigoneka masana.

Nanga ndizingokhala ndili zunguliruzunguliru

ku magulu a ziŵeto za abusa anzako!

Mwamuna

8Iwe wokongola koposa akazi onsewe,

ngati sukukudziŵa,

uzingotsata m'makwalala a msambi wa ziŵeto,

uzidyetsa mbuzi zako pambali pa mahema a abusawo.

9Iwe bwenzi langa,

kukongola kwako, ngati akavalo a magaleta a Farao.

10Masaya ako akukongola

ndi ndolo zam'makutuzi.

Khosi lakonso likukongola

ndi mikanda ya miyala yamtengowapatali.

11Tidzakupangira ukufu wagolide,

wokhala ndi timakaka tasiliva.

Mkazi

12Pamene mfumu inali gone podyera pake,

mafuta anga onunkhira adapereka kafungo kachikoka.

13Wokondedwa wanga ndikumuwona

ngati kathumba ka mure,

kamene kamakhala pakati pa maŵere angaŵa.

14Wokondedwa wanga ndikumuwona

ngati chipukutu cha maluŵa ofiira

a m'munda wamphesa wa ku Engedi.

Mwamuna

15Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongola,

ndiwe chiphadzuŵa.

Maso ako akunga ngati nkhunda.

Mkazi

16Wokondedwa wanga, nawenso ndiwe wokongola,

wokongoladi zedi.

Malo athu ogonapo ndi msipu wobiriŵira.

17Mitanda ya nyumba yathu ndi yamkungudza,

phaso lake ndi la mtengo wa paini.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help