Mas. 56 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pemphero losonyeza kukhulupirira MulunguKwa Woimbitsa Nyimbo. Kutsata maimbidwe a nyimbo yoti: Njiŵa yatera m'mitengo ya thundu yakutali. Salmo la Davide la mtundu wa Mikitamu. Afilisti anali atamugwira ku Gati.

1Inu Mulungu, mundichitire chifundo,

pakuti anthu akundizunza.

Adani akundithira nkhondo ndi kundipsinja tsiku lonse.

2Adani akundizunza tsiku lonse,

pali ambiri amene akumenyana nane monyada.

3Pamene ndichita mantha ndimadalira Inu.

4Ndimatamanda Mulungu chifukwa cha zimene wandilonjeza.

Ndimakhulupirira Mulungu mopanda mantha.

Kodi munthu angandichite chiyani?

5Tsiku lonse adaniwo amafunafuna

kulepheretsa zolinga zanga.

Zonse zimene amaganiza ndi zoti andichite zoipa.

6Amasonkhana okhaokha namabisalira,

amalonda mayendedwe anga,

amafuna kundipha.

7Muŵalange chifukwa cha zoipa zao.

Inu Mulungu, muŵakwiyire anthuwo ndi kuŵaononga.

8Inu mwaona kupiripita kwanga,

mudziŵa kuchuluka kwa misozi yanga.

Kodi zonsezi sizidalembedwe m'buku lanu?

9Tsono adani anga adzabwezedwa m'mbuyo

pa tsiku lomwe ndidzaitana Mulungu.

Ndikudziŵa kuti Mulungu ali pa mbali yanga.

10Ndimatamanda Mulungu chifukwa cha mau ake.

Ndimatamanda Chauta chifukwa cha zimene wandilonjeza.

11Ndimadalira Mulungu, sindidzachita mantha konse.

Kodi munthu angandichite chiyani?

12Ndiyenera kuchita zimene ndidalumbira kwa Inu Mulungu.

Ndidzapereka kwa Inu nsembe zothokozera.

13Pakuti mwalanditsa moyo wanga ku imfa.

Inde mwandichirikiza mapazi kuti ndisagwe,

kuti motero ndiziyenda pamaso pa Mulungu

m'kuŵala kwa amoyo.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help