Mas. 78 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mulungu ndi anthu ake.Ndakatulo ya Asafu.

1Mvetsetsani zimene ndikukuphunzitsani,

inu anthu anga.

Tcherani khutu, mumve mau a pakamwa panga.

2 Mt. 13.35 Ndidzakusimbirani fanizo.

Ndidzalankhula nkhani zobisika zakalekale,

3zinthu zimene tidazimva ndi kuzidziŵa,

zomwe makolo athu adatifotokozera.

4Sitidzabisira ana ao,

koma tidzafotokozera mbadwo wakutsogolo

ntchito zotamandika za Chauta,

tidzaŵasimbira mphamvu zake ndi zodabwitsa

zimene wakhala akuchita.

5Adapereka mau odzichitira umboni kwa Yakobe,

adakhazikitsa malamulo ake mu Israele.

Adalamula makolo athu

kuti aziŵaphunzitsa ana ao malamulowo.

6Motero mbadwo wakutsogolo wa ana amene sanabadwebe,

udzaŵadziŵa,

ndipo nawonso udzafotokozera ana ake.

7Anawo aike chikhulupiriro chao pa Mulungu,

ndipo asaiŵale ntchito za Mulungu,

koma asunge malamulo ake.

8Asakhale ngati makolo ao,

anthu oukira ndi osamvera aja,

mbadwo wa anthu amene mitima yao inali yosakhazikika,

amene moyo wao unali wosakhulupirika kwa Mulungu.

9Ngakhale Aefuremu anali ndi mauta,

komabe adathaŵa pa tsiku la nkhondo,

10sadasunge chipangano cha Mulungu,

koma adakana kutsata malamulo ake.

11Iwo adaiŵala zimene Mulungu adachita,

ndiponso zozizwitsa zimene Iye adaŵaonetsa.

12 Eks. 7.8—12.32 Mulungu adachita zodabwitsa zake,

makolo ao akuwona,

m'dziko la Ejipito, ku dera la Zowani.

13 Eks. 14.21, 22 Adagaŵa nyanja pakati, kuti iwo apitepo,

ndipo adaimiritsa madzi ngati makoma.

14 Eks. 13.21, 22 Masana ankaŵatsogolera ndi mitambo,

usiku ankaŵatsogolera ndi kuŵala kwamoto.

15Adang'amba matanthwe am'chipululu,

naŵapatsa madzi ochuluka ngati amumtsinje,

kuti amwe.

16 Lun. 16.1—19.22 Eks. 17.1-7; Num. 20.2-13 Adatumphutsa mifuleni m'thanthwe,

nayendetsa madzi ngati mitsinje.

17Komabe iwo adapitiriza kumchimwira,

naukira Mulungu Wopambanazonse m'chipululu muja.

18 Eks. 16.2-15; Num. 11.4-23, 31-35 Iwo adayesa Mulungu m'mitima mwao,

pomuumiriza kuti aŵapatse chakudya chimene ankakhumba.

19Adalankhula motsutsana ndi Mulungu nati,

“Kodi Mulungu angathe kutipatsa chakudya

m'chipululu muno?

20Paja adamenya thanthwe,

kotero kuti madzi adatumphuka,

ndipo mitsinje idadzaza.

Kodi angathenso kutipatsa ife anthu ake buledi

kapena kutipezera nyama?”

21Nchifukwa chake Chauta atamva zimenezi,

adapsa mtima kwambiri,

adayatsira moto Yakobe,

napambana kukwiyira Israeleyo,

22popeza kuti sadadalire Mulungu,

sadakhulupirire mphamvu zake zopulumutsa.

23Komabe Iye adalamula mitambo yamumlengalenga,

natsekula zitseko zakumwamba.

24 Lun. 16.20-29; Yoh. 6.31 Poŵagwetsera mana kuti adye,

adaŵapatsa tirigu wakumwamba.

25Motero anthu adadya buledi wa angelo,

ndipo Mulungu adaŵatumizira chakudya chochuluka.

26Adakunthitsa mphepo yakuvuma mu mlengalenga,

adatulutsa mphepo yakumwera ndi mphamvu zake.

27Adaŵagwetsera nyama yochuluka ngati fumbi,

mbalame zochuluka ngati mchenga wakunyanja.

28Adalola kuti zigwere pakati pa zithando zao,

konsekonse kumalo kumene ankakhalako.

29Motero adadya nakhuta kwambiri,

popeza kuti adaŵapatsa zakudya zimene ankakhumba.

30Koma nkhuli yao isanathe,

asanameze nkumeza komwe chakudya chaocho,

31mkwiyo wa Mulungu udaŵayakira,

ndipo adapha amphamvu onse pakati pao,

adapha anyamata abwinoabwino onse a mu Israele.

32Ngakhale zinali chomwecho,

iwo adapitirirabe kuchimwa,

sadakhulupirire ngakhale adaona zodabwitsa zake.

33Choncho Mulungu adadula masiku ao

kuti azimirire ngati mpweya,

adadula zaka zao

kuti zithere m'zoopsa.

34Pamene ankapha ena,

otsalira ankayamba kumufunafuna.

Ankalapa namafunafuna Mulungu ndi mtima wao wonse.

35Adakumbukira kuti Mulungu ndi thanthwe loŵateteza,

kuti Mulungu Wopambanazonse ndiye Mpulumutsi wao.

36Koma iwo adamthyasika ndi pakamwa pao,

adamnamiza ndi lilime lao.

37 Ntc. 8.21 Mtima wao sunali wokhulupirika kwa Iye.

Sadasunge chipangano chake.

38Komabe pakuti Mulungu ngwachifundo,

adaŵakhululukira machimo ao,

ndipo sadaŵaononge.

Kaŵirikaŵiri ankadziletsa kukwiya,

sadalole kuti mkwiyo wake wonse uyake.

39Ankakumbukira kuti iwo anali anthu chabe,

ngati mphepo yopita imene siibwereranso.

40Kaŵirikaŵiri ankamuukira m'chipululu,

ankamumvetsa chisoni.

41Kaŵirikaŵiri ankamuyesa,

ankamputa Woyera wa Israele.

42Sadakumbukire mphamvu zake

kapena tsiku limene adaŵaombola kwa adani ao,

43pamene Iye adachita zizindikiro zamphamvu ku Ejipito,

ndiponso zozizwitsa zake ku dera la ku Zowani.

44 Eks. 7.17-21 Paja Mulungu adasandutsa madzi a mitsinje yao

kuti akhale magazi,

kotero kuti Aejipito sadathe kumwa madziwo.

45 Eks. 8.20-24; Eks. 8.1-6 Adaŵatumira nthenje za ntchentche

zimene zidaŵazunza,

ndiponso achule amene adasakaza dziko lao.

46 Eks. 10.12-15 Adalola kuti kapuchi adye mbeu zao

ndiponso kuti dzombe lidye zonse za m'minda mwao.

47 Eks. 9.22-25 Adaononga mphesa zao ndi matalala

ndiponso mitengo yao yankhuyu ndi chisanu.

48Adalola kuti ng'ombe zao zife ndi matalala

ndi kuti nkhosa zao zife ndi zing'aning'ani.

49Adagwetsa moto wa ukali wake pa iwo:

adaŵapsera mtima naŵakwiyira

nkuŵagwetsera mavuto.

Zimenezi zinali ngati gulu la angelo oononga.

50Adalola kukwiya, osadziletsa,

sadaŵapulumutse ku imfa,

koma adapereka moyo wao ku miliri.

51 Eks. 12.29 Adapha ana achisamba onse a Aejipito,

ana oyamba a mphamvu zao,

m'zithando za zidzukulu za Hamu.

52 Eks. 13.17-22 Tsono Mulungu adaŵatulutsa anthu ake ngati nkhosa,

naŵatsogolera m'chipululu ngati zoŵeta.

53 Eks. 14.26-28 Adaŵatsogolera bwino lomwe

kotero kuti sanalikuwopa,

koma nyanja idamiza adani ao.

54 Eks. 15.17; Yos. 3.14-17 Adaŵafikitsa ku dziko lake loyera,

ku dziko lamapiri limene adaŵagonjetsera

ndi dzanja lake lamphamvu.

55 Yos. 11.16-23 Adapirikitsa mitundu ina ya anthu,

kuŵachotsa m'njira.

Adagaŵagaŵa dziko la anthuwo kuti likhale la anthu ake,

adakhazikitsa mafuko a Israele m'midzi ya anthuwo.

56 Owe. 2.11-15 Komabe Aisraele adamuputa

ndi kumuukira Mulungu Wopambanazonse,

sadasunge malamulo ake,

57koma iwo adakhala okanika ndi osakhulupirika

monga makolo ao.

Adapotoka ngati uta wosakhulupirika.

58Iwo adakwiyitsa Mulungu

ndi akachisi ao opembedzerako mafano ku mapiri.

Adamupsetsa mtima chifukwa cha mafano ao osemawo.

59Pamene Mulungu adamva zimenezi,

adakwiya kwambiri,

ndipo adakana Aisraele kotheratu.

60 Yos. 18.1; Yer. 7.12-14; 26.6 Adasiya malo ake a Silo kumene ankakhala,

adasiya hema limene ankakhalamo pakati pa anthu,

61 1Sam. 4.4-22 ndipo adalola adani athu

kuti alande Bokosi la Chipangano chake,

limene linali chizindikiro cha mphamvu zake

ndi ulemerero wake.

62Chifukwa adakwiyira anthu ake,

adalola kuti anthu akewo aphedwe pa nkhondo.

63Nkhondo yoyaka ngati moto idaononga anyamata ao,

ndipo atsikana ao adasoŵa oŵaimbira nyimbo zaukwati.

64Ansembe ao omwe adaphedwa ndi lupanga,

ndipo akazi ao amasiye sadaŵalole kulira maliro.

65Pomaliza Ambuye adachita ngati kudzuka kutulo,

ngati munthu wamphamvu wofuula chifukwa choledzera.

66Tsono Mulungu adaŵapirikitsa adani ake,

naŵachititsa manyazi anthaŵizonse.

67Adakana banja la Yosefe,

sadasankhule fuko la Efuremu.

68Koma adasankhula fuko la Yuda,

ndiponso phiri la Ziyoni limene amalikonda.

69Adamanga malo ake opatulika

ngati malo ake akumwamba,

okhazikika ngati dziko lapansi mpaka muyaya.

70 1Sam. 16.11, 12; 2Sam. 7.8; 1Mbi. 17.7 Mulungu adasankhula Davide mtumiki wake,

ndipo adakamtenga ku makola a nkhosa.

71Adamtenga kumene ankaŵeta nkhosa

zimene zinali ndi ana,

kuti adzakhale mbusa wa Yakobe, fuko lake,

wa Israele, choloŵa chake.

72Davide adaŵasamala ndi mtima wolungama,

naŵatsogolera ndi dzanja lake mwaluso.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help