Mas. 125 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mulungu ateteza anthu akeNyimbo yoimba pokwera ku Yerusalemu.

1Anthu amene amakhulupirira Chauta

ndi olimba ngati phiri la Ziyoni,

limene silingathe kugwedezeka,

koma ndi lokhala mpaka muyaya.

2Monga momwe mapiri amazingira Yerusalemu,

momwemonso Chauta akuzinga anthu ake

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

3Mafumu oipa sadzalamulira nthaƔi yonse

dziko limene lapatsidwa kwa anthu ake,

kuti nawonso anthu olungamawo angachite zoipa.

4Chauta, achitireni zabwino

anthu amene ali abwino,

amene ali olungama mtima.

5Koma anthu amene amatsata njira zao zokhotakhota,

Chauta adzaƔapirikitsira

kumene kuli anthu ochita zoipa.

Mtendere ukhale ndi Israele.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help