Miy. 21 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wa madzi

m'manja mwa Chauta.

Amauwongolera ku zimene Iyeyo akufuna.

2Makhalidwe a munthu amakhala olungama

pamaso pa mwiniwakeyo,

koma Chauta ndiye amayesa mtima wake.

3Kuchita zolungama ndi zokhulupirika

kumakondweretsa Chauta koposa kupereka nsembe.

4Maso odzikuza ndi mtima wonyada

zimatsogolera anthu oipa ngati nyale,

nchifukwa chake amachimwa.

5Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa dzinthu dzake,

koma aliyense wochita zinthu mofulumira udyo,

amangokhala wosoŵa.

6Chuma chomachipeza monyenga

chimangoti wuzi ngati nthunzi,

ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.

7Ndeu za anthu oipa zidzaŵaononga,

poti amakana kuchita zolungama.

8Njira ya munthu woipa ndi yokhotakhota,

koma khalidwe la munthu wosachimwa ndi lolungama.

9 Mphu. 25.16 Kuli bwino kukhala potero pa denga

kupambana kukhala m'nyumba

pamodzi ndi mkazi wolongolola.

10Mtima wa munthu woipa umalakalaka zoipa.

Samva chifundo konse ndi mnzake wovutika.

11Munthu wonyoza akalangidwa,

wopusapusa amaphunzirapo nzeru.

Munthu wanzeru akamlangiza, amamvetsa zambiri.

12Mulungu ngwachilungamo nthaŵi zonse,

amadziŵa zimene anthu oipa akuchita

ndipo adzawaononga.

13Amene amatseka m'khutu wosauka akamalira,

adzalira iyenso,

koma kulira kwakeko sikudzamveka.

14Mphatso yam'seri imaposa ukali,

ndipo chiphuphu chosereza chimathetsa

mphamvu ngakhale ya mkwiyo woopsa.

15Chilungamo chikachitika,

nzika zabwino zimakondwera,

koma zimadederetsa atambwali.

16Munthu amene amasiya njira ya anthu anzeru,

adzapezeka m'gulu la anthu akufa.

17Amene amakondetsa zosangalatsa,

adzasanduka munthu wosauka.

Amene amakondetsa vinyo ndi mafuta, sadzalemera.

18Oipa adzakhala choombolera anthu abwino,

ndipo osakhulupirika adzakhala choombolera anthu

a mtima wabwino.

19Kuli bwino kukhala ku chipululu

kupambana kukhala ndi mkazi wolongolola

ndi wopsa mtima msanga.

20Munthu wanzeru samwaza chuma chake,

koma munthu wopusa amachiwononga.

21Amene amatsata chilungamo ndi

chifundo adzapeza moyo ndi ulemu.

22Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu a mphamvu,

ndipo amagwetsa linga lamphamvu

limene anthuwo ankalikhulupirira.

23Amene amagwira pakamwa ndi kusamala zokamba zake,

sapeza mavuto.

24Munthu wonyada ndi wodzikuza amamtchula “Mnyodoli,”

chifukwa amachita zinthu modzitama ndi mwachipongwe.

25Kulakalaka kwa munthu waulesi kumamupha,

poti amangokhala manja ali khoba, osagwira ntchito.

26Tsiku lathunthu anthu oipa amasirira zinthu,

koma omvera Mulungu amapatsa ndipo alibe kaliwumira.

27 Mphu. 7.9 Nsembe ya anthu oipa imamnyansa Chauta,

nanji tsono akaipereka ndi cholinga choipa!

28Mboni yonama idzaonongeka,

koma mau a munthu wakumva adzamveka nthaŵi zonse.

29Munthu woipa amafuna kuwoneka wolimba mtima,

koma munthu woongoka amaganizira bwino zochita zake.

30Palibe nzeru, palibe kumvetsa zinthu,

palibe ngakhale uphungu,

zimene zingathe kupambana Chauta.

31Kavalo amamkonzera tsiku la nkhondo,

koma ndi Chauta amene amapambanitsa.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help