Mas. 65 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Za kutamanda ndi kuthokozaKwa Woimbitsa Nyimbo. Salmo la Davide; Nyimbo.

1Inu Mulungu, anthu azikutamandani ku Ziyoni,

achitedi zimene adalumbira kwa Inu.

2Inu amene mumamvera pemphero,

anthu onse adzabwera kwa Inu,

3chifukwa cha machimo ao.

Pamene zochimwa zathu zitipambana,

Inu mumazifafaniza.

4Ngwodala munthu amene Inu mumamsankha

nkubwera naye kudzakhala m'mabwalo anu.

Mutikhutitse ndi zinthu zabwino za m'Nyumba yanu,

Nyumba yanu yoyera.

5Tsono Inu mumatiyankha

potipulumutsa ndi ntchito zanu zodabwitsa,

Inu Mulungu Mpulumutsi wathu.

Anthu a pa dziko lonse lapansi

ndiponso a patsidya pa nyanja zakutali,

onsewo amakhulupirira Inu.

6Inu mudaonetsa mphamvu zanu,

pokhazikitsa mapiri.

7Inu mumachititsa bata mkokomo wa nyanja

ndi mkokomo wa mafunde

ndi phokoso la mitundu ina ya anthu.

8Motero okhala ku malire akutali a dziko lapansi

amaopa zizindikiro zanu zodabwitsa.

Anthu amafuula mokondwera chifukwa cha zochita zanu,

kuyambira mbali imodzi ya dziko lapansi

mpaka mbali yake inanso.

9Tsono Inu mumadalitsa dziko lapansi ndi kulithirira,

ndipo mumalilemeza kwambiri.

Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi,

Inu mumaŵapatsa anthu dzinthu,

pakuti ndimo m'mene mwalikonzera dzikolo.

10Inu mumathirira kwambiri makwaŵa am'mizere,

mumasalaza nthumbira zake,

mumafeŵetsa nthaka ndi mvula,

ndipo mumadalitsa mbeu.

11Pakutha pa chaka mumapereka zokolola zambiri

mwa ubwino wanu,

kulikonse kumene Inu mupita,

kumapezeka dzinthu dzambiri.

12Ngakhale ku mabusa akuchipululu

kumamera msipu wambiri,

ndipo mapiri amadzazidwa ndi chimwemwe.

13Madambo adzaza ndi zoŵeta,

zidikha zadzaza ndi dzinthu,

zonsezo zikufuula ndi kuimbira limodzi mwachimwemwe.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help