Yes. 62 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Za ulemerero wa Yerusalemu

1Chifukwa chokonda Ziyoni

sindidzakhala chete,

chifukwa chokonda Yerusalemu

sindidzakhala chete,

mpaka chilungamo chake

chitaoneka poyera ngati kuŵala,

ndipo chipulumutso chake

chitaoneka ngati muuni woyaka.

2Iwe Yerusalemu,

mitundu ya anthu idzakuwona utapambana pa nkhondo,

mafumu ao onse adzaona ulemerero wako.

Adzakuitanira dzina latsopano,

limene adzakutche ndi Chauta yemwe.

3Udzakhala ngati chisoti chaufumu

chokongola m'manja mwa Chauta,

ngati nsangamutu yaulemerero

m'manja mwa Mulungu wako.

4Sudzatchedwanso “Wosiyidwa,”

dziko lako silidzatchedwanso “Chipululu.”

Dzina lako latsopanolo lidzakhala “Ndikukondwera naye.”

Dziko lako lidzatchedwa “Wokwatiwa mwachimwemwe,”

chifukwa choti Chauta akukondwera nawe,

ndipo adzakhala ngati mwamuna wa dziko lako.

5Monga mnyamata amakwatira namwali,

chonchonso mmisiri wodzakumanganso adzakukwatira.

Monganso mkwati wamwamuna amakondwerera mkwati wamkazi,

chonchonso Mulungu adzasangalala nawe.

6Iwe Yerusalemu,

pa malinga ako ndaikapo alonda,

usana wonse ndi usiku wonse sadzakhala chete.

Inu amene mumakumbutsa Chauta za malonjezo ake,

musapumule.

7Musaleke kumkumbutsa mpaka atakhazikitsanso Yerusalemu,

ndi kuusandutsa mzinda umene dziko lapansi lidzautamanda.

8Chauta adalumbira motsimikiza,

ndipo adzasunga malumbirowo ndi mphamvu zake.

Adati, “Adani ako sadzadyanso tirigu wako,

ndipo alendo sadzamwanso vinyo wako.

9Koma inu amene mudabzala ndi kukolola tiriguyo,

ndiye amene mudzadye buledi,

ndipo mudzatamanda Chauta.

Inu amene munkasamala mitengo yamphesa

ndi kumathyola mphesa,

ndiye amene mudzamwe vinyo m'mabwalo a Nyumba yanga.”

10Tulukani, inu a mu Yerusalemu,

inde tulukani mumzindamo,

mukakonze mseu woti anthu anu obwerera kwao aziyendamo.

Mulambule mseu waukulu, ndipo muchotsemo miyala.

Mukweze mbendera kuti mitundu ya anthu iziwona.

11 Yes. 40.10; Chiv. 22.12 Chauta walengeza ku dziko lonse lapansi

zakuti muuze anthu a ku Yerusalemu kuti,

“Chipulumutso chanu chikubwera.

Chauta akubwera ndi mphotho yake,

akubwera nazo zokuyenererani.

12Mudzatchedwa anthu opatulika a Mulungu,

anthu amene Chauta waŵapulumutsa.

Iwe Yerusalemu,

udzatchedwa Mzinda wokondedwa wa Chauta,

mzinda umene Mulungu sadausiye.”

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help