Mas. 52 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Za chiweruzo cha Mulungu ndi kukoma mtima kwakeKwa Woimbitsa Nyimbo. Ndakatulo ya Davide. Doegi Mwedomu anali atakauza Saulo kuti, “Davide wapita kwa Ahimeleki.”

1Bwanji ukunyadira ntchito zako zoipa,

munthu wamphamvuwe?

2Tsiku lonse umakhalira kusinkhasinkha za kuwononga ena,

lilime lako lili ngati lumo lakuthwa,

ntchito yako nkunyenga.

3Umakonda zoipa kupambana zabwino,

umakonda kunama kupambana kulankhula zoona.

4Umakonda kulankhula mau ovutitsa ena,

iwe wabodzawe.

5Koma Mulungu adzakutswanya kosalekeza,

adzakugwira ndi kukutulutsira kunja kwa nyumba yako.

Adzakuzula m'dziko la anthu amoyo.

6Anthu ochita zachilungamo adzaona zimenezi,

ndipo adzachita mantha.

Adzakuseka ndi kumanena kuti,

7“Muwoneni munthu amene sadafune kudalira Mulungu,

koma adakhulupirira chuma chake chochuluka,

nalimbikira kuchita zoipa.”

8Koma ine ndili ngati mtengo wauŵisi wa olivi

m'Nyumba ya Mulungu.

Ndimaika mtima nthaŵi zonse

pa chikondi chosasinthika cha Mulungu.

9Ndidzakuthokozani Inu Mulungu mpaka muyaya,

chifukwa cha zimene mwachita.

Ndidzatamanda dzina lanu pamaso pa anthu okukondani,

pakuti ndinu abwino.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help