Mas. 124 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mulungu Mpulumutsi wa anthu akeNyimbo ya Davide yoimba pokwera ku Yerusalemu.

1Chauta akadapanda kukhala pa mbali yathu,

Israele anene choncho tsopano,

2Chauta akadapanda kukhala pa mbali yathu,

pamene anthu adatiwukira,

3bwenzi atatimeza amoyo,

muja mkwiyo wao udatiyakira,

4bwenzi chigumula chitatisesa,

madzi amkokomo atatikokolola,

5bwenzi madzi amphamvu atatimiza.

6Atamandike Chauta,

amene sadatipereke kwa anthuwo kuti atiwononge.

7Taonjoka ngati mbalame

mu msampha wa osaka,

msampha wathyoka, ndipo ife tapulumuka.

8Chithandizo chathu chimachokera kwa Chauta,

amene adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help