1Mzimu wanu wosafa umakhala m'zinthu zonse.
2Nchifukwa chake anthu akakunyozani,
mumaŵalanga pang'onopang'ono.
Mumaŵakumbutsa machimo ao ndi kuŵachenjeza
kuti asiye zoipa ndi kukhulupirira Inu, Ambuye.
Mulungu alanga Akanani3 Deut. 12.31; 18.9-13 Anthu akale amene ankakhala m'dziko lanu loyera
4mudadana nawo chifukwa cha zochita zao zonyansa,
chifukwa cha zaufiti ndi miyambo ina yoipa.
5Ankapha ana mopanda chifundo,
pa maphwando ao a nsembe zao
ankadya nyama ya anthu
ndi kumamwa magazi ao.
Adaphunzitsidwa miyambo yonyansadi,
6anakubala ankapha ana opanda chitetezo.
Inuyo mudagamula zoti makolo athu
aononge anthu amenewo,
7kuti dziko limene munkalikonda
kupambana maiko onse,
lilandire fuko loyenera la ana a Mulungu.
8 Eks. 23.28 Komabe popeza kuti adaniwo anali anthu,
mudaŵachitira chifundo.
Ankhondo anu asanafike,
mudatsogoza mavu ambiri
kuti akaononge adaniwo pang'onopang'ono.
9Kunali kotheka kwa Inu kuwononga anthu osamverawo
pakuŵayambanitsa nkhondo ndi anthu olungama,
kapena kuŵatsiriza onse kamodzinkamodzi ndi zilombo,
kapenanso ndi mau anu amodzi okha mopanda chisoni.
10 2Es. 9.11 Koma poŵalanga pang'onopang'ono,
mudaŵapatsa mpata wolapira,
chifukwa munkadziŵa bwino
kuti adabadwa m'machimo.
Kuipa kwao kunali kwachibadwa,
ndipo maganizo ao anali osasinthika.
11Unali mtundu wotembereredwa chiyambire.
Ngakhale mudaaŵalekerera machimo ao osaŵalanga,
sichinali chifukwa choopa wina aliyense ai.
Mulungu ndi wamphamvuzonse12Ndani angakufunseni kuti,
“Kodi mwachita chiyani?”
Ndani angatsutsepo pa zogamula zanu?
Ndani angakuimbeni mlandu
chifukwa choti mwaononga mitundu ya anthu
imene inu nomwe mudailenga?
Ndani angabwere pamaso panu
kudzaŵalankhulira mau oteteza anthu osamveraŵa?
13Pajatu Mulungu ndinu nokha, palibenso wina.
Ndinu nokha amene mumasamala anthu onse.
Palibenso wina amene muyenera kumufotokozera
ngati chigamulo chanu ndi cholungama.
14Palibenso mfumu kapena muweruzi wina
amene angathe kukudzudzulani
pa za anthu amene mudaŵalanga.
15Ndinu olungama,
mumayendetsa zinthu zonse molungama.
Kwa Inu sizikugwirizana konse ndi mphamvu zanu
kuti mulange munthu wosayenera kulangidwa.
16Mphamvu zanu ndiye gwero la chilungamo chanu,
choncho popeza kuti ndinu mwini anthu onse,
mumaŵachitira chifundo onse.
17Anthu amene amakayika
kuti ndinu Mulungu Wamphamvuzonse,
mumaŵaonetsa mphamvu zanu.
Anthu amene amadziŵa zimenezi
nkukuchitanibe chipongwe,
mumaŵachititsa manyazi.
18Koma ngakhale ndinu mwini mphamvu,
mumaweruza mofatsa.
Mumatilamula ndi mtima wachifundo,
poti mukangofuna,
mumaonetsa mphamvu zanu.
Mulungu atiwonetsa phindu la kupirira19Pochita ntchito zanu zoterezi,
mudaphunzitsa anthu anu kuti wolungama ayenera
kukhala wachifundo,
mudadzaza ana anu ndi chikhulupiriro,
chifukwa mumakhululukira anthu ochimwa.
20Ngati adani a ana anu mudaŵalanga mofatsa
ndi moleza mtima,
ngakhale ankayenera kuphedwa,
mudaŵapatsa nthaŵi yosiya machimo ao pakutero,
21nanji tsono ana anu,
iwowo mudaŵaweruza mosamala kopambana,
Inu amene mudapereka kwa makolo ao
malonjezo anu ndi chipangano chanu
kuti mudzaŵapatsa madalitso ochuluka.
22Ife mukamatilanga,
adani mumaŵasautsa moŵirikiza,
kuti tizilingalira bwino za chifundo chanu
pamene tikuweruza ena,
kuti Inu podzatiweruza,
tidzathe kudalira chifundo chanu.
Mulungu alanga Aejipito23Tsono anthu openga aja,
amene anali ndi makhalidwe oipa,
mudaŵalanga ndi zoipa zao zomwe.
24Iwo adasokera kwambiri ndi njira zao zonama,
kotero kuti nyama zoipa ndi zonyansa kwambiri
ankaziyesa milungu.
Ankangokhulupirira zopusa
ngati ana opanda nzeru.
25Nchifukwa chake iwowo
pokhala ngati ana opanda nzeru,
mudaŵatumizira chilango chanu
choŵaonetsa kuti ndi opusa.
26Koma amene sadasamaleko madzudzulo ochenjezawo,
adzalandira chilango choyenera kwa Mulungu.
27Mutaŵalanga nazo zolengedwa
zimene adaaziyesa milungu zija,
adapsa nazo mtima zoŵazunzazo.
Adaona ndi kuzindikira kuti
Chauta ndiye Mulungu woona,
Iye amene iwo adaakana kumuvomera.
Nchifukwa chake chilango choopsa chidaaŵagwera.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.