Mas. 53 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Za kuipa kwa anthu(Mas. 14)Kwa Woimbitsa Nyimbo. Kutsata maimbidwe a nyimbo yoti: Pa matenda. Ndakatulo ya Davide.

1 Aro. 3.10-12 Mumtima mwake munthu wopusa amati,

“Kulibe Mulungu.”

Anthu otereŵa ndi oipa,

amachita zonyansa,

palibe ndi mmodzi yemwe wochita zabwino.

2Mulungu kumwambako waŵerama,

akuyang'ana anthu pansi pano,

kuti aone ngati angakhalepo mmodzi wanzeru

wofunitsitsa Mulungu.

3Koma ai anthu onse ndi osokera,

onsewo ndi oipa chimodzimodzi.

Palibe ndi mmodzi yemwe wochita zabwino,

ai, palibiretu ndi mmodzi yemwe.

4Kani anthu oipaŵa alibe nzeru chotere?

Iwo amameza anthu anga, kuŵayesa chakudya,

ndipo samutama Mulungu mopemba.

5Tsonotu iwo adzachita mantha aakulu,

mantha ake amene sadaoneke ndi kale lonse.

Pakuti Mulungu adzaononga adani okuzingani.

Inu mudzaŵachititsa manyazi

chifukwa Mulungu waŵakana.

6Chibwere ndithu chipulumutso cha Israele

kuchokera ku Ziyoni!

Mulungu akadzaŵabwezera ufulu anthu ake,

Yakobe adzakondwera,

Israele adzasangalala kwambiri.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help