Yes. 17 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Za kudzalangidwa kwa Damasiko ndi Efuremu

1 kapena maguwa ofukizapo lubani.

9Tsiku limenelo mizinda yamphamvu ya Aisraele idzasiyidwa monga mizinda ya Aamori ndi ya Ahivi imene anthu adaaisiya pothaŵa Aisraelewo. Ndipo idzakhala mabwinja.

10Inu Aisraele, mwaiŵala Mulungu Mpulumutsi wanu,

simudamkumbukire Iye

amene ndiye thanthwe lokupulumutsani.

M'malo mwake, mumabzala mbeu zabwino,

kubzalira milungu yachilendo,

11Mumati zikule tsiku lomwe mwabzalalo,

mumati zituluke maluŵa m'maŵa momwe mwazibzalamo,

komabe zimene mudzakololezo

zidzatha pa tsiku lamavuto,

ndipo mazunzo ake adzakhala osatha.

Adani agonjetsedwa

12Ha, anthu a mitundu yambiri

akusokosa kwambiri!

Phokoso lao lili ngati kukokoma kwa nyanja!

Ha, lumbwe la anthu a mitundu ina,

likusokosa ngati madzi amphamvu!

13Ankhondo a mitundu ina akubwera

ndi mkokomo ngati wa madzi ambiri.

Koma Mulungu akuŵadzudzula,

ndipo iwo adzathaŵira kutali.

Adzapirikitsidwa ngati mankhusu

ouluka ndi mphepo pa mapiri,

ngati fumbi la kamvulumvulu namondwe asanayambe.

14Pa nthaŵi yamadzulo ndi oopsa!

Koma kusanache, onse azimirira.

Umu ndimo m'mene zidzaŵachitire

anthu otilanda zathu.

Limeneli ndilo tsoka la anthu otibera zinthu zathu.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help