Mas. 131 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pemphero la munthu wokhulupirira modzichepetsaNyimbo ya Davide yoimba pokwera ku Yerusalemu.

1Chauta, mtima wanga ndi wosadzikuza,

maso anga ndi osanyada.

Sinditengeka mtima ndi zinthu zapamwamba ndi zodabwitsa.

2Koma ndautonthoza ndi kuukhalitsa chete mtima wanga,

monga mwana amene mai wake amamtonthoza ndi bere.

Momwemo mtima wanga uli phe m'kati mwanga.

3Iwe Israele, khulupirira Chauta

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help