Mas. 122 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kutamanda YerusalemuNyimbo ya Davide yoimba pokwera ku Yerusalemu.

1Ndidasangalala pamene adandiwuza kuti,

“Tiyeni tipite ku Nyumba ya Chauta.”

2Mapazi athu akhala akuima m'kati mwa zipata zako,

iwe Yerusalemu.

3Yerusalemu adamangidwa bwino,

zigawo zake zonse nzogwirizana pamodzi.

4Kumeneko kumapita mafuko onse,

anthu ake a Chauta,

monga momwe adalamulira Israele

kuti akayamike dzina la Chauta.

5Kumeneko adaikako mipando yaufumu yoweruzira,

mipando yake ya banja la Davide.

6Pemphererani mtendere wa Yerusalemu ponena kuti,

“Anthu amene amakukonda iwe Yerusalemu,

zinthu ziziŵayendera bwino.

7Mtendere ukhale m'kati mwa makoma ako,

bata likhale m'nyumba zako zachifumu.”

8Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga

ndidzanena kuti,

“Mtendere ukhaledi m'kati mwako.”

9Chifukwa cha Nyumba ya Chauta, Mulungu wathu,

ndidzakupemphera zabwino.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help