Mas. 75 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mulungu woweruzaKwa Woimbitsa Nyimbo. Kutsata maimbidwe a nyimbo yoti: Musaononge. Salmo la Asafu.

1Tikukuthokozani Inu Mulungu,

ndithu tikukuthokozani.

Tikutchula dzina lanu mopemphera

ndipo tikulalika ntchito zanu zodabwitsa.

2Inu mukuti, “Pa nthaŵi imene ndiisankhule,

ndidzaweruza mwachilungamo.

3Pamene dziko lapansi likugwedezeka

pamodzi ndi zonse zokhalamo,

ndine amene ndimachirikiza mizati yake.”

4Ndimauza anthu odzitama kuti, “Musadzitame,”

ndiponso anthu oipa kuti,

“Musadzitukumule chifukwa cha mphamvu zanu.

5Musadzikuze chifukwa cha mphamvu zanu,

kapena kumalankhula zamwano.”

6Kugamula milandu sikuchokeratu kuvuma kapena kuzambwe,

ndiponso sikuchokera ku chipululu.

7Koma ndi Mulungu yekha amene amagamula milandu,

amatsitsa wina, nakweza wina.

8M'manja mwa Chauta mulitu chikho cha vinyo

wofanizira chilango chake,

vinyo wotutuma ndi wothirako dzoŵaŵa.

Adzatsanyula vinyoyo,

ndipo oipa onse a pa dziko lapansi adzamwa,

nadzagugudiza mpaka ndungundungu zake.

9Koma ine sindidzaleka kukondwera,

ndidzaimba nyimbo zotamanda Mulungu wa Yakobe

mpaka muyaya.

10Iye adzaphwanya mphamvu za anthu onse oipa,

koma adzaonjezera mphamvu za anthu okhulupirira.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help