Mas. 137 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Madandaulo a Aisraele m'dziko lachilendo

1M'mbali mwa mitsinje ya ku Babiloni,

kumeneko tidakhala pansi

nkumalira tikukumbukira Ziyoni.

2Kumeneko tidapachika apangwe athu

pa mitengo ya misondodzi.

3Kumeneko anthu otigwira ukapolo adatipempha

kuti tiimbe nyimbo.

Otizunza adatipempha

kuti tisangalale,

adati,

“Tatiimbiraniko nyimbo ya ku Ziyoni.”

4Tsono ife tidati,

“Tingaimbe bwanji nyimbo ya Chauta

kuchilendo ngati kuno?”

5Ndikakuiŵala iwe Yerusalemu,

dzanja langa lamanja liwume.

6Lilime langa likangamire

ku mnakanaka m'kamwa mwanga,

ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu

ndi kukuwona kuti ndiwe wondisangalatsa kwambiri.

7Kumbukirani, Inu Chauta,

zimene adachita Aedomu

pa tsiku lija la kuwonongeka kwa Yerusalemu,

muja ankati,

“Mgwetseni pansi, mgwetseni pansi,

mpaka pa maziko ake.”

8 Chiv. 18.6 Mzinda wa Babiloni, iwe woyenera kuwonongedwawe,

adzakhala wodala munthu amene adzakubwezera

zimene watichita ifezi.

9Adzakhala wodala munthu amene adzatenga makanda ako

ndi kuŵakankhanthitsa ku thanthwe.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help