Mas. 4 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pemphero lamadzulo lopempha chithandizoKwa Woimbitsa Nyimbo. Aimbire zazingwe. Salmo la Davide.

1Ndikamaitana,

mundiyankhe Inu Mulungu, Mtetezi wanga.

Mudabwera kudzandithandiza

pamene ndinali m'mavuto.

Mundichitire chifundo, ndi kumvera pemphero langa.

2Anthu inu, mudzaleka liti kunyoza ulemu wanga?

Bwanji mukukondabe zinthu zachabechabe?

Bwanji mukulakalakabe zinthu zonama?

3Koma tsono mudziŵe

kuti Chauta wadzipatulira Iye yemwe anthu olungama.

Chauta amamva ndikamuitana.

4 Aef. 4.26 Opani Mulungu, ndipo musachimwe.

Mukhale phee ndipo muganize zimenezi mu mtima

pamene mukugona.

5Perekani nsembe zanu ndi mtima wolungama,

ikani mitima yanu pa Chauta.

6Alipo ambiri amene amati,

“Ndani angatiwonetse zabwino?

Mutiyang'ane ndi chikondi chanu, Inu Chauta.”

7Koma Inu mwandisangalatsa mtima kwambiri,

kupambana anthu a zakudya ndi zakumwa zambiri!

8Choncho ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere,

pakuti Inu nokha Chauta

ndinu amene mumandisunga bwino lomwe.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help