1Inu Mulungu, imvani kulira kwanga,
mverani pemphero langa.
2Ine wokhala ku mathero a dziko lapansi,
ndataya mtima, ndipo ndikuitana Inu.
Munditsogolere ku thanthwe lalitali.
3Inutu ndinu kothaŵira kwanga,
nsanja yolimba yonditeteza kwa adani.
4Mundilole ndizikhala m'Nyumba mwanu nthaŵi zonse.
Mundilole ndibisale pansi pa mapiko anu
kuti munditeteze.
5Inu Mulungu, mwamva zimene ndalumbira popemphera.
Inu mwandipatsa choloŵa
chimene amalandira anthu oopa dzina lanu.
6Talikitsani moyo wa mfumu,
zaka zake zifikire ku mibadwo ndi mibadwo.
7Akhale pa mpando wake waufumu
pamaso pa Mulungu mpaka muyaya.
Inu Chauta, mumsunge mokhulupirika
chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
8Motero nthaŵi zonse
ndidzaimba nyimbo zotamanda dzina lanu,
tsiku ndi tsiku ndidzachitadi zimene ndidalumbirazo.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.