Mphu. 1 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

ZONENA ZANZERUChiyambi cha nzeru ndi makhalidwe ake

1 Miy. 2.6 Nzeru zilizonse nzochokera kwa Ambuye,

zimakhala ndi Iwo nthaŵi zonse.

2Ndani angaŵerenge mchenga wakunyanja?

Ndani angaŵerenge madontho a mvula?

Ndipo ndani angaŵerenge masiku a muyaya?

3Ndani angathe kuyesa kutalika kwa mlengalenga?

Ndani angayese kukula kwa dziko lapansi?

Ndani angayese kuzama kwa phompho?

Nanji tsono ndani angayese kuzama kwa nzeru?

4Nzeru ndizo zinali zoyamba kulengedwa,

zinthu zina zilizonse zisanalengedwe.

Kumvetsa zinthu mwanzeru kudaalipo chiyambire.

5Kasupe wa nzeru ndi mau a Mulungu

amene ali kumwamba.

Makhalidwe ake ndi malamulo amuyaya.

6Maziko a nzeru ndani adamuululirapo?

Nanga kuchenjera kwake ndani amakudziŵa?

7Ndani amadziŵa zonse zimene nzeru zimadziŵa?

Ndani amamvetsa zonse zimene nzeru zimamvetsa?

8Alipo Mmodzi yekha wanzeru,

woyenera kumamuwopa kwambiri,

wokhala pa mpando wake waufumu.

Ameneyo ndi Ambuye.

9 Miy. 8.22-31; Mphu. 24.9 Ndiwo amene adalenga nzeru,

adaziyang'ana ndi kuziyesa

ndipo adaziika m'ntchito zake zonse.

10Nzeruzo zimakhala mwa anthu

ngati mphatso ya Mulungu,

ndipo Iyeyo amazipatsa amene amamkonda.

Za Kuwopa Mulungu

11Kuwopa Ambuye kumapatsa ulemerero

ndi chikondwerero,

kumapatsa chimwemwe

ndi nsangamutu ya chisangalalo.

12Kuwopa Ambuye kumakondweretsa mtima,

kumapatsa chisangalalo,

chimwemwe ndi moyo wautali.

13Amene amaopa Ambuye,

zonse zidzamuyendera bwino mpaka ku mathero.

Mulungu adzamdalitsa pa tsiku la kufa kwake.

14Kuwopa Ambuye ndiye chiyambi cha nzeru.

Anthu okhulupirika amazilandira

akali m'mimba mwa amai ao.

15Zimakhazikika pakati pa anthu mpaka muyaya,

ndipo zidzukulu za anthuwo

zidzadalira nzeru zimenezo.

16Kuwopa Ambuye ndiye nzeru zenizeni,

anthu amakhuta ndi zipatso zake.

17 Lun. 7.11 Nzeru zimadzaza nyumba za anthu

ndi zimene iwo akufuna,

nkhokwe zao zimadzaza ndi zokolola zake.

18Kuwopa Ambuye ndiye nzeru zonse zathunthu,

kumapatsa mtendere ndi moyo wamphamvu.

19Nzeru zimathandiza kudziŵa

ndi kumvetsa zinthu.

Onse amene ali nazo nzeruzo,

zimaŵakulitsira ulemerero wao.

20 Miy. 3.16; 4.10 Kuwopa Ambuye ndiye maziko a nzeru,

nthambi zake ndi moyo wautali.

21Kuwopa Ambuye kumachotsa machimo;

pamene nzeru zakhazikika,

mkwiyo umathaŵapo.

22Kukwiya popanda chifukwa

sikungakhale chinthu cholungama.

Mkwiyo umaononga mwiniwake yemwe.

23Munthu wopirira amadzigwira

mpaka nthaŵi yake yoyenera itafika,

pambuyo pake amadzakondwera kwabasi.

24Mau ake amaŵasunga mu mtima,

mpaka nthaŵi yake itafika.

Pambuyo pake anthu amadzakamba

zoti munthuyo ngwanzeru.

25Nzeru zili ndi malangizo okhwima

m'nkhokwe mwake,

koma kukonda zachipembedzo

munthu woipa kumamunyansa.

26Ukafuna nzeru, tsata malamulo,

apo Ambuye adzakupatsadi nzeruzo.

27Kuwopa Ambuye

ndiye nzeru ndi kusunga mwambo.

Kukhulupirika ndi kufatsa

ndiye zimene zimakondweretsa Ambuyewo.

28Usanyozere za kuwopa Ambuye,

usaŵayandikire Ambuyewo ndi mtima wonyenga.

29Usakhale wachiphamaso pakati pa anthu,

ndipo uzisamala bwino mau ako.

30Usadzitame kuwopa kuti ungagwe nuchita manyazi,

Ambuye nkuulula zinsinsi zako

ndi kukuchititsa manyazi pamaso pa anthu,

chifukwa mayendedwe ako sanali oopa Ambuyewo.

Mtima wako unali wonyenga kwambiri.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help