Mas. 142 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pemphero lopempha chithandizoNdakatulo ya Davide.Adainena ngati pemphero, pamene anali m'phanga.

1Ndikulirira Chauta mokweza,

ndikupemba kwa Chauta mofuula.

2Ndikupereka madandaulo anga kwa Iye,

ndikutchula mavuto anga pamaso pake.

3Pamene mtima wanga ufooka,

Inu mumadziŵa zoti ndichite.

Adani anditchera msampha

m'njira imene ndimayendamo.

4Ndikayang'ana ku dzanja lamanja,

palibe ndi mmodzi yemwe wosamalako za ine.

Kulibe koti ndithaŵire,

palibe munthu wondisamala.

5Ndimalirira Inu Chauta,

ndimati, “Inu ndinu kothaŵira kwanga,

ndinu zanga zonse m'dziko la amoyo.”

6Imvani kulira kwanga,

pakuti ndataya mtima.

Pulumutseni kwa ondizunza,

chifukwa andiposa mphamvu.

7Tulutseni m'ndende

kuti ndizitamanda dzina lanu.

Anthu anu adzandizungulira,

chifukwa Inu mwandichitira zabwino zambiri.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help