YAKOBO 1 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

1 Yoh. 7.35; Mac. 12.17; 26.7; 1Pet. 1.1 Yakobo, kapolo wa Mulungu ndi wa Ambuye Yesu Khristu, kwa mafuko khumi ndi awiri a m'chibalaliko: ndikupatsani moni.

Za mayesero

2 1Pet. 1.6 Muchiyese chimwemwe chokha, abale anga, m'mene mukugwa m'mayesero a mitundumitundu;

3Aro. 5.3pozindikira kuti chiyesedwe cha chikhulupiriro chanu chichita chipiriro.

4Koma chipiriro chikhale nayo ntchito yake yangwiro, kuti mukakhale angwiro ndi opanda chilema, osasowa kanthu konse.

5 Miy. 2.3-6; Mat. 7.7 Koma wina wa inu ikamsowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, amene apatsa kwa onse modzala manja, niwosatonza; ndipo adzampatsa iye.

6Mrk. 11.24Koma apemphe ndi chikhulupiriro, wosakayika konse; pakuti wokayikayo afanana ndi funde la nyanja lotengeka ndi mphepo ndi kuwinduka nayo.

7Pakuti asayese munthu uyu kuti adzalandira kanthu kwa Ambuye;

8munthu wa mitima iwiri akhala wosinkhasinkha panjira zake zonse.

9Koma mbale woluluka adzitamandire pa ukulu wake;

10Mas. 90.5-6ndipo mbale wolemera anyadire pamene atsitsidwa, pakuti adzapita monga duwa la udzu.

11Pakuti latuluka dzuwa ndi kutentha kwake, ndipo laumitsa udzu; ndipo lathothoka duwa lake, ndi ukoma wa maonekedwe ake waonongeka; koteronso wachuma adzafota m'mayendedwe ake.

12 1Ako. 10.13; 2Tim. 4.8; 2Pet. 2.9 Wodala munthu wakupirira poyesedwa; pakuti pamene wavomerezeka, adzalandira korona wa moyo, amene Ambuye adalonjezera iwo akumkonda Iye.

13Munthu poyesedwa, asanena, Ndiyesedwa ndi Mulungu; pakuti Mulungu sangathe kuyesedwa ndi zoipa, ndipo Iye mwini sayesa munthu:

14koma munthu aliyense ayesedwa pamene chilakolako chake cha iye mwini chimkokera, ndikumnyenga.

15Mas. 7.14; Aro. 6.23Pamenepo chilakolakocho chitaima, chibala uchimo; ndipo uchimo, utakula msinkhu, ubala imfa.

16Musanyengedwe, abale anga okondedwa.

17Mala. 3.6; 1Ako. 4.7Mphatso iliyonse yabwino, ndi chininkho chilichonse changwiro zichokera Kumwamba, zotsika kwa Atate wa mauniko, amene alibe chisanduliko, kapena mthunzi wa chitembenukiro.

18Yoh. 1.13; Chiv. 14.4Mwa chifuniro chake mwini anatibala ife ndi mau a choonadi, kuti tikhale ife ngati zipatso zoyamba za zolengedwa zake.

Tikhale akuchita a mau

19 Miy. 14.17; Mlal. 5.1 Mudziwa, abale anga okondedwa, kuti munthu aliyense akhale wotchera khutu, wodekha polankhula, wodekha pakupsa mtima.

20Pakuti mkwiyo wa munthu suchita chilungamo cha Mulungu.

21Aef. 1.13; Akol. 3.8Mwa ichi, mutavula chinyanso chonse ndi chisefukiro cha choipa, landirani ndi chifatso mau ookedwa mwa inu, okhoza kupulumutsa moyo wanu.

22Mat. 7.21Khalani akuchita mau, osati akumva okha, ndi kudzinyenga nokha.

23Luk. 6.49Pakuti ngati munthu ali wakumva mau, wosati wakuchita, iyeyu afanana ndi munthu wakuyang'anira nkhope yake ya chibadwidwe chake m'kalirole;

24pakuti wadziyang'anira yekha, nachoka, naiwala pompaja nali wotani.

25Koma iye wakupenyerera m'lamulo langwiro, ndilo laufulu, natero chipenyerere, ameneyo, posakhala wakumva wakuiwala, komatu wakuchita ntchito, adzakhala wodala m'kuchita kwake.

26Mas. 34.13Ngati wina adziyesera ali wopembedza Mulungu, ndiye wosamanga lilime lake, koma adzinyenga mtima wake, kupembedza kwake kwa munthuyu nkopanda pake.

27Mat. 25.36; 1Yoh. 5.18Mapembedzedwe oyera ndi osadetsa pamaso pa Mulungu ndi Atate ndiwo: kucheza ndi ana amasiye ndi akazi amasiye m'chisautso chao, ndi kudzisungira mwini wosachitidwa mawanga ndi dziko lapansi.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help