MASALIMO 137 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Kudandaula kwa Ayuda ku Babiloni

1Ku mitsinje ya ku Babiloni,

kumeneko tinakhala pansi, inde tinalira,

pokumbukira Ziyoni.

2Pa msondodzi uli m'mwemo

tinapachika mazeze athu.

3Popeza pamenepo akutigwirawo anatifunsa nyimbo

ndipo akutizunza anafuna tisekere,

ndi kuti, Mutiimbire nyimbo imodzi ya ku Ziyoni.

4 Neh. 2.3 Tidati, Tidzaimba bwanji nyimbo ya Yehova

m'dziko lachilendo?

5Ndikakuiwalani, Yerusalemu,

dzanja lamanja langa liiwale luso lake.

6 Ezk. 3.26 Lilime langa limamatike kunsaya zanga,

ndikapanda kukumbukira inu;

ndikapanda kusankha Yerusalemu

koposa chimwemwe changa chopambana.

7 Yer. 49.7-10; Ezk. 25.12 Yehova, kumbukirani ana a Edomu

tsiku la Yerusalemu;

amene adati, Gamulani, gamulani,

kufikira maziko ake.

8 Yes. 13.1-22 Mwana wamkazi wa ku Babiloni,

iwe amene udzapasulidwa;

wodala iye amene adzakubwezera chilango

monga umo unatichitira ife.

9Wodala iye amene adzagwira makanda ako,

ndi kuwaphwanya pathanthwe.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help