MASALIMO 85 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Akumbutsa Mulungu madalitso akale, apempha awabwerezeKwa Mkulu wa Nyimbo: Salimo la ana a Kora.

1 Ezr. 1.11 Munachita zovomereza dziko lanu, Yehova;

munabweza ukapolo wa Yakobo.

2 Mas. 32.1 Munachotsa mphulupulu ya anthu anu,

munafotsera zolakwa zao zonse.

3Munabweza kuzaza kwanu konse;

munabwerera kumkwiyo wanu wotentha.

4Mutibweze, Mulungu wa chipulumutso chathu,

nimuletse udani wanu wa pa ife.

5 Mas. 74.1 Kodi mudzatikwiyira nthawi zonse?

Kodi mudzakhala chikwiyire mibadwomibadwo?

6 Hab. 3.2 Kodi simudzatipatsanso moyo,

kuti anthu anu akondwerere ndi Inu?

7Tionetseni chifundo chanu, Yehova,

tipatseni chipulumutso chanu.

8 Hab. 2.1; Zek. 9.10 Ndidzamva cholankhula Mulungu Yehova;

pakuti adzalankhula zamtendere ndi anthu ake,

ndi okondedwa ake;

koma asabwererenso kuchita zopusa.

9 Yes. 46.13 Indedi chipulumutso chake chili pafupi

ndi iwo akumuopa Iye;

kuti m'dziko mwathu mukhale ulemu.

10 Yes. 32.17 Chifundo ndi choonadi zakomanizana;

chilungamo ndi mtendere zapsompsonana.

11 Yes. 45.8 Choonadi chiphukira m'dziko;

ndi chilungamo chasuzumira chili m'mwamba.

12 Mas. 67.6 Inde Yehova adzapereka zokoma;

ndipo dziko lathu lidzapereka zipatso zake.

13 Mas. 89.14 Chilungamo chidzamtsogolera;

ndipo chidzamkonzera mapazi ake njira.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help