1 TIMOTEO 2 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Pemphero la kwa anthu onse

1Ndidandaulira tsono, poyambayamba, kuti achitike mapembedzo, mapemphero, mapembedzero, mayamiko, chifukwa cha anthu onse;

2Ezr. 6.10; Yer. 29.7chifukwa cha mafumu ndi onse akuchita ulamuliro; kuti m'moyo mwathu tikakhale odika mtima ndi achete m'kulemekeza Mulungu, ndi m'kulemekezeka monse.

3Pakuti ichi nchokoma ndi cholandirika pamaso pa Mulungu Mpulumutsi wathu;

4Yoh. 3.16-17amene afuna anthu onse apulumuke, nafike pozindikira choonadi.

5Aro. 3.29-30; Aheb. 8.6Pakuti pali Mulungu mmodzi, ndi Mtetezi mmodzi pakati pa Mulungu ndi anthu, ndiye munthu, Khristu Yesu,

6Mrk. 10.45amene anadzipereka yekha chiombolo m'malo mwa onse; umboni m'nyengo zake;

7Aef. 3.7umene anandiika ine mlaliki wake ndi mtumwi (ndinena zoona, wosanama ine), mphunzitsi wa amitundu m'chikhulupiriro ndi choonadi.

8 Mas. 134.2; Yes. 1.15; Mala. 1.11; Yoh. 4.21 Chifukwa chake ndifuna kuti amunawo apemphere pamalo ponse, ndi kukweza manja oyera, opanda mkwiyo ndi makani.

Zoyenera akazi

9 1Pet. 3.3-4 Momwemonso, akazi adziveke okha ndi chovala choyenera, ndi manyazi, ndi chidziletso; osati ndi tsitsi lake loluka, ndi golide kapena ngale, kapena malaya a mtengo wake wapatali;

101Pet. 3.3-4komatu (umo mokomera akazi akuvomereza kulemekeza Mulungu), mwa ntchito zabwino.

11Mkazi aphunzire akhale wachete m'kumvera konse.

121Ako. 14.34; Aef. 5.24Koma sindilola ine kuti mkazi aphunzitse, kapena kulamulira mwamuna; komatu akhale chete.

13Pakuti Adamu anayamba kulengedwa, pamenepo Heva;

14Gen. 3.6ndipo Adamu sananyengedwe, koma mkaziyo ponyengedwa analowa m'kulakwa;

15koma adzapulumutsidwa mwa kubala mwana, ngati akhala m'chikhulupiriro ndi chikondi ndi chiyeretso pamodzi ndi chidziletso.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help