MIYAMBO 4 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Chenjezo lakuti afune Nzeru nalewe njira za oipa

1Ananu, mverani mwambo wa atate,

nimutchere makutu mukadziwe luntha;

2pakuti ndikuphunzitsani zabwino;

musasiye chilangizo changa.

3 1Mbi. 29.1 Pakuti ndinali mwana kwa atate wanga,

wokondedwa ndi mai, ndine ndekha, sanabale wina.

4Atate nandiphunzitsa, nati kwa ine,

mtima wako uumirire mau anga;

sunga malamulo anga, nukhale ndi moyo.

5Tenga nzeru, tenga luntha;

usaiwale, usapatuke pa mau a m'kamwa mwanga;

6usasiye nzeru, ndipo idzakusunga;

uikonde, idzakutchinjiriza.

7Nzeru ipambana, tatenga nzeru;

m'kutenga kwako konseko utenge luntha.

8Uilemekeze, ndipo idzakukweza;

idzakutengera ulemu pamene uifungatira.

9Idzaika chisada cha chisomo pamutu pako;

idzakupatsa korona wokongola.

10Tamvera mwananga, nulandire mau anga;

ndipo zaka za moyo wako zidzachuluka.

11Ndakuphunzitsa m'njira ya nzeru,

ndakuyendetsa m'mayendedwe olungama.

12Mapazi ako sadzaombana ulikuyenda;

ukathamanga, sudzaphunthwa.

13Gwira mwambo, osauleka;

uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.

14 Mas. 1.1 Usalowe m'mayendedwe ochimwa,

usayende m'njira ya oipa.

15Pewapo, osapitamo;

patukapo, nupitirire.

16 Yes. 57.20 Pakuti akapanda kuchita zoipa, samagona;

ndipo akapanda kukhumudwitsa wina, tulo tao tiwachokera.

17Pakuti amadya chakudya cha uchimo,

namwa vinyo wa chifwamba.

18 2Sam. 23.2, 4; Mat. 5.14-16 Koma mayendedwe a olungama akunga kuunika kwa mbandakucha,

kunkabe kuwala kufikira usana woti mbee.

19 1Sam. 2.9 Njira ya oipa ikunga mdima;

sadziwa chimene chiwaphunthwitsa.

20Mwananga, tamvera mau anga;

tcherera makutu ku zonena zanga.

21Asachoke kumaso ako;

uwasunge m'kati mwa mtima wako.

22 Deut. 32.46-47 Pakuti ali moyo kwa omwe awapeza,

nalamitsa thupi lao lonse.

23Chinjiriza mtima wako koposa zonse uzisunga;

pakuti magwero a moyo atulukamo.

24Tasiya m'kamwa mokhota,

uike patali milomo yopotoka.

25Maso ako ayang'ane m'tsogolo,

zikope zako zipenye moongoka.

26Sinkhasinkha bwino mayendedwe a mapazi ako;

njira zako zonse zikonzeke.

27 Yos. 1.7 Usapatuke kudzanja lamanja kapena kulamanzere;

suntha phazi lako kusiya zoipa.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help