MIYAMBO 13 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

1 1Sam. 2.24-25 Mwana wanzeru amamvera mwambo wa atate;

koma wonyoza samvera chidzudzulo.

2Munthu adzadya zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwake;

koma moyo wa achiwembu udzadya chiwawa.

3 Yak. 3.2 Wogwira pakamwa pake asunga moyo wake;

koma woyasamula milomo yake adzaonongeka.

4Moyo wa waulesi ukhumba osalandira kanthu;

koma moyo wa akhama udzalemera.

5Wolungama ada mau onama;

koma woipa anyansa, nadzichititsa manyazi.

6Chilungamo chitchinjiriza woongoka m'njira;

koma udyo ugwetsa wochimwa.

7Alipo wodziyesa wolemera, koma alibe kanthu;

alipo wodziyesa wosauka, koma ali ndi chuma chambiri.

8Chiombolo cha moyo wa munthu ndicho chuma chake;

koma wosauka samva chidzudzulo.

9Kuunika kwa olungama kukondwa;

koma nyali ya oipa idzazima.

10Kudzikuza kupikisanitsa;

koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.

11Chuma cholandiridwa mokangaza chidzachepa;

koma wokundika ndi dzanja adzaona zochuluka.

12Chiyembekezo chozengereza chidwalitsa mtima;

koma pakufika chifunirocho ndicho mtengo wa moyo.

13 2Mbi. 36.16 Wonyoza mau adziononga yekha;

koma woopa malangizo adzalandira mphotho.

14 2Sam. 22.6-7 Malamulo a wanzeru ndiwo kasupe wa moyo,

apatutsa kumisampha ya imfa.

15Nzeru yabwino ipatsa chisomo;

koma njira ya achiwembu ili makolokoto.

16Yense wochenjera amachita mwanzeru;

koma wopusa aonetsa utsiru.

17Mthenga wolakwa umagwa m'zoipa;

koma mtumiki wokhulupirika alamitsa.

18Wokana mwambo adzasauka nanyozedwa;

koma wolabadira chidzudzulo adzalemekezedwa.

19Chifuniro chikondweretsa moyo chitachitidwa;

koma kusiya zoipa kunyansa opusa.

20Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru:

koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.

21 Mas. 32.10 Zoipa zilondola ochimwa;

koma olungama adzalandira mphotho yabwino.

22Wabwino asiyira zidzukulu zake cholowa chabwino;

koma wochimwa angosungira wolungama chuma chake.

23M'kulima kwa osauka muli zakudya zambiri;

koma zinazo zimaonongeka posowa chiweruzo.

24 Miy. 23.13 Wolekerera mwanake osammenya amuda;

koma womkonda amyambize kumlanga.

25 Mas. 34.10 Wolungama adya nakhutitsa moyo wake;

koma mimba ya oipa idzasowa.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help