MASALIMO 67 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Amitundu alemekeze MulunguKwa Mkulu wa Nyimbo, pa Neginoto. Salimo. Nyimbo.

1 Num. 6.25 Atichitire chifundo Mulungu, ndi kutidalitsa,

atiwalitsire nkhope yake;

2 Luk. 2.30, 41 kuti njira yanu idziwike padziko lapansi,

chipulumutso chanu mwa amitundu onse.

3Anthu akuyamikeni, Mulungu;

anthu onse akuyamikeni.

4 96.10, 13 Anthu akondwere, nafuule mokondwera;

pakuti mudzaweruza anthu molunjika,

ndipo mudzalangiza anthu padziko lapansi.

5Anthu akuyamikeni, Mulungu;

anthu onse akuyamikeni.

6 Lev. 26.4 Dziko lapansi lapereka zipatso zake,

Mulungu, Mulungu wathu adzatidalitsa.

7 Mas. 22.27 Mulungu adzatidalitsa;

ndipo malekezero onse a dziko lapansi adzamuopa Iye.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help